Yobu
8 Bilidadi+ wa ku Shuwa+ anayankha kuti:
2 “Kodi ukhala ukulankhula chonchi mpaka liti?+
Mawu a mʼkamwa mwako ali ngati mphepo yamphamvu.
3 Kodi Mulungu angapotoze chilungamo?
Kapena kodi Wamphamvuyonse angapotoze zinthu zimene ndi zolungama?
4 Ngati ana ako anamuchimwira,
Iye anawalanga chifukwa cha kupanduka kwawo,*
5 Koma ngati iweyo utayangʼana kwa Mulungu,+
Nʼkuchonderera Wamphamvuyonse kuti akuchitire chifundo,
6 Ndipo ngati ukanakhaladi woyera komanso ngati umachitadi zoyenera,+
Iye akanakumvera*
Ndipo akanakubwezeretsa mmene unalili poyamba.
9 Chifukwa ife tabadwa dzulodzuloli, ndipo sitikudziwa kalikonse,
Chifukwa masiku athu padziko lapansi ali ngati mthunzi.
11 Kodi gumbwa* angamere pamalo pamene si padambo?
Ndipo kodi bango lingakule popanda madzi?
12 Lidakali ndi maluwa, lisanadulidwe nʼkomwe,
Lidzauma zomera zonse zisanaume.
13 Zimenezi ndi zimene zidzachitikire* anthu onse amene aiwala Mulungu,
Chifukwa chiyembekezo cha anthu oipa* chidzatha,
14 Anthu amene amadalira zinthu zosathandiza,
Amene amadalira zinthu zosalimba ngati ulusi wa kangaude.*
15 Iye adzatsamira nyumba yake, koma idzagwa.
Adzayesetsa kuigwira, koma sidzalimba.
17 Mizu yake imapiringizana pamulu wa miyala.
Iye amaona kuti miyalayo ndi nyumba yake.
20 Ndithudi, Mulungu sadzakana anthu okhulupirika,*
Kapena kuthandiza* anthu ochita zoipa.
21 Chifukwa adzakupangitsa kuti useke,
Ndipo udzafuulanso chifukwa chosangalala.
22 Anthu odana nawe adzachita manyazi,
Ndipo tenti ya anthu oipa kudzakhala kulibe.”