Yobu
16 Yobu anayankha kuti:
2 “Ndamvapo zinthu zambiri ngati zimenezi.
Nonsenu ndinu otonthoza obweretsa mavuto!+
3 Kodi simusiya kulankhula mawu opanda pakewa?*
Chikukupwetekani nʼchiyani kuti muziyankha chonchi?
4 Inenso ndikanatha kulankhula ngati mmene mukuchitiramu.
Mukanakhala kuti mukukumana ndi mavuto ngati angawa,*
Ndikanalankhula mawu ambiri okudzudzulani
Komanso kukupukusirani mutu.+
5 Koma sindikanatero, mʼmalomwake ndikanakulimbikitsani ndi mawu amʼkamwa mwanga,
Ndipo mawu otonthoza apakamwa panga akanakulimbikitsani.+
8 Komanso iye wandigwira ndipo anthu ena akuona zimenezi,
Moti kuwonda kwangaku ndi umboni wonditsutsa.
9 Mkwiyo wa Mulungu wandikhadzula ndipo akundisungira chidani.+
Iye akundikukutira mano.
Mdani wanga akundiyangʼana mokwiya nʼcholinga choti andivulaze.+
10 Anthu atsegula kukamwa kwawo kuti andimeze.+
Ndipo andimenya mbama pofuna kundichititsa manyazi.
Iwo asonkhana ambirimbiri kuti alimbane nane.+
12 Ine ndinali pa mtendere koma iye wandiphwanya.+
Wandigwira kumbuyo kwa khosi nʼkundimenyetsa pansi,
Kenako wandiponyera mivi yake.
13 Anthu ake oponya mivi ndi uta andizungulira.+
Iye waboola impso zanga+ ndipo sakumva chisoni,
Wakhuthulira ndulu yanga pansi.
14 Iye akungokhalira kundiboola ngati khoma.
Akundithamangira ngati msilikali.
16 Nkhope yanga yafiira chifukwa cholira,+
Ndipo pazikope zanga pali mdima wandiweyani,*
17 Ngakhale kuti manja anga sanachite zachiwawa,
Ndipo pemphero langa ndi loyera.
18 Iwe dziko lapansi, usabise magazi anga.+
Alole kuti alire mʼmalo mwa ine.
19 Ngakhale panopa, mboni yanga ili kumwamba,
Amene angandichitire umboni ali mʼmwamba.