Yobu
26 Yobu anayankha kuti:
2 “Komatu ndiye wathandiza munthu wopanda mphamvu!
Wapulumutsa munthu wa manja ofooka.+
3 Waperekadi malangizo othandiza kwa munthu wopanda nzeru.+
Komanso wachititsa kuti anthu ambiri adziwe nzeru zothandiza.
5 Akufa alibe mphamvu ndipo amanjenjemera pamaso pa Mulungu.
Iwo ali pansi kwambiri kuposa madzi ndi zonse zimene zimakhala mmenemo.
7 Iye anatambasula thambo lakumpoto* pamwamba pa malo opanda kanthu,+
Ndipo dziko lapansi analiika mʼmalere.
8 Iye anakulunga madzi mʼmitambo yake,+
Mʼnjira yoti mitamboyo isaphulike chifukwa cha kulemera kwa madziwo.
9 Anaphimba mpando wake wachifumu kuti usamaoneke,
Anauphimba ndi mtambo wake.+
11 Zipilala zakumwamba zimanjenjemera,
Zimachita mantha ndi kudzudzula kwa Mulungu.
12 Ndi mphamvu zake amavundula nyanja,+
Ndipo ndi kuzindikira kwake amaduladula chilombo cha mʼnyanja.*+
13 Ndi mpweya umene wapuma,* amapangitsa kuti kumwamba kukhale koyera.
Dzanja lake limabaya njoka yothamanga.
14 Komatu zimenezi ndi kambali kakangʼono chabe ka zochita zake,+
Ndipo tangomva kunongʼona kwapansipansi kwa mphamvu zake.
Ndiye ndi ndani amene angamvetse mabingu ake amphamvu?”+