Salimo
Nyimbo ndi Salimo la ana a Kora.+
48 Yehova ndi wamkulu komanso woyenera kutamandidwa kwambiri,
Mumzinda wa Mulungu wathu, mʼphiri lake loyera.
2 Phiri la Ziyoni limene lili mʼdera lakutali lakumpoto,
Ndi lokongola chifukwa lili pamalo okwezeka komanso anthu padziko lonse lapansi akusangalala nalo,+
Ndipo ndi mzinda wa Mfumu Yaikulu.+
3 Munsanja zake zokhala ndi mpanda wolimba,
5 Iwo ataona mzindawo, anadabwa.
Anapanikizika nʼkuthawa mwamantha.
6 Kumeneko iwo anayamba kunjenjemera,
Anavutika ngati mkazi amene akubereka.
7 Pogwiritsa ntchito mphepo yamphamvu yakumʼmawa, munaswa sitima za ku Tarisi.
8 Zimene tinangomva, tsopano taziona tokha,
Mumzinda wa Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, mumzinda wa Mulungu wathu.
Mulungu adzakhazikitsa mzindawo mpaka kalekale.+ (Selah)
Dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.+
13 Ganizirani mofatsa za mpanda wake wolimba.+
Yenderani nsanja zake zokhala ndi mpanda wolimba,
Kuti mudzafotokozere mibadwo yamʼtsogolo.