Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Machitidwe 23
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Zimene Zili Mʼbuku la Machitidwe

      • Paulo analankhula pamaso pa Khoti Lalikulu la Ayuda (1-10)

      • Paulo analimbikitsidwa ndi Ambuye (11)

      • Chiwembu chofuna kupha Paulo (12-22)

      • Paulo anapititsidwa ku Kaisareya (23-35)

Machitidwe 23:1

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 24:15, 16; 2Ak 1:12; Ahe 13:18; 1Pe 3:16

Machitidwe 23:2

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kuchitira Umboni Mokwanira, tsa. 187

Machitidwe 23:5

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 22:28

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kuchitira Umboni Mokwanira, tsa. 187

    Nsanja ya Olonda,

    11/1/2002, tsa. 5

    6/15/1990, tsa. 23

Machitidwe 23:6

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 26:4, 5; Afi 3:4, 5

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kuchitira Umboni Mokwanira, ptsa. 187-188

    Nsanja ya Olonda,

    4/15/2005, tsa. 31

Machitidwe 23:8

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 4:1, 2

Machitidwe 23:9

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 22:6, 7, 17, 18

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kuchitira Umboni Mokwanira, tsa. 188

Machitidwe 23:11

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 18:9
  • +Mac 27:23, 24; 28:23, 30, 31

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kuchitira Umboni Mokwanira, ptsa. 189-191

    Nsanja ya Olonda (Yophunzira),

    11/2020, tsa. 13

    Nsanja ya Olonda,

    6/15/1990, tsa. 24

    8/1/1987, tsa. 14

Machitidwe 23:12

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kuchitira Umboni Mokwanira, tsa. 191

Machitidwe 23:16

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Utumiki Komanso Moyo Wathu,

    1/2019, tsa. 3

Machitidwe 23:20

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 23:15

Machitidwe 23:21

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 23:12

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kuchitira Umboni Mokwanira, ptsa. 190-191

Machitidwe 23:23

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “ola lachitatu,” kuwerenga kuchokera 6 koloko madzulo.

  • *

    Ena amati “mahosi.”

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kuchitira Umboni Mokwanira, tsa. 191

Machitidwe 23:25

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    12/15/2001, tsa. 22

Machitidwe 23:27

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 21:31-33
  • +Mac 16:37; 22:25

Machitidwe 23:28

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 22:30

Machitidwe 23:29

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 25:19

Machitidwe 23:30

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 23:16

Machitidwe 23:31

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 23:23, 24

Machitidwe 23:34

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 21:39; 22:3

Machitidwe 23:35

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 24:1

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Mac. 23:1Mac 24:15, 16; 2Ak 1:12; Ahe 13:18; 1Pe 3:16
Mac. 23:5Eks 22:28
Mac. 23:6Mac 26:4, 5; Afi 3:4, 5
Mac. 23:8Mac 4:1, 2
Mac. 23:9Mac 22:6, 7, 17, 18
Mac. 23:11Mac 18:9
Mac. 23:11Mac 27:23, 24; 28:23, 30, 31
Mac. 23:20Mac 23:15
Mac. 23:21Mac 23:12
Mac. 23:27Mac 21:31-33
Mac. 23:27Mac 16:37; 22:25
Mac. 23:28Mac 22:30
Mac. 23:29Mac 25:19
Mac. 23:30Mac 23:16
Mac. 23:31Mac 23:23, 24
Mac. 23:34Mac 21:39; 22:3
Mac. 23:35Mac 24:1
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
  • 26
  • 27
  • 28
  • 29
  • 30
  • 31
  • 32
  • 33
  • 34
  • 35
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Machitidwe 23:1-35

Machitidwe a Atumwi

23 Paulo anayangʼanitsitsa Khoti Lalikulu la Ayudalo nʼkunena kuti: “Anthu inu, abale anga, ndachita zinthu popanda chikumbumtima changa kunditsutsa ngakhale pangʼono pamaso pa Mulungu+ mpaka lero.” 2 Hananiya mkulu wa ansembe atamva zimenezi, analamula anthu amene anaimirira pafupi naye kuti amʼmenye pakamwa. 3 Atatero, Paulo anamuuza kuti: “Uona, Mulungu akulanga, khoma lopaka laimu iwe. Wakhala pamenepo kuti undiweruze motsatira Chilamulo, ndiye ukuphwanyanso Chilamulocho polamula kuti andimenye?” 4 Anthu amene anaima naye pafupi anati: “Kodi ukunyoza mkulu wa ansembe wa Mulungu?” 5 Paulo anati: “Abale, sindinadziwe kuti ndi mkulu wa ansembe. Chifukwa Malemba amati, ‘Wolamulira wa anthu a mtundu wako usamunenere zachipongwe.’”+

6 Paulo ataona kuti ena a iwo anali Asaduki ndipo ena anali Afarisi, anafuula mʼkhotimo kuti: “Anthu inu, abale anga, ine ndine Mfarisi,+ mwana wa Afarisi. Pano ndikuweruzidwa chifukwa cha chiyembekezo chakuti akufa adzauka.” 7 Atanena zimenezi, Afarisi ndi Asaduki anayamba kukangana kwambiri, ndipo gululo linagawanika. 8 Chifukwa Asaduki amanena kuti munthu wakufa sangauke komanso kulibe angelo kapena cholengedwa chauzimu. Pomwe Afarisi amavomereza poyera kuti zonsezi zilipo.+ 9 Choncho panali chiphokoso, ndipo alembi ena a gulu la Afarisi anaimirira nʼkuyamba kutsutsa mwaukali kuti: “Sitikupeza chimene munthuyu walakwa. Koma ngati mzimu kapena mngelo walankhula naye+ . . .” 10 Mkanganowo utakula kwambiri, mkulu wa asilikali anachita mantha kuti anthuwo amukhadzulakhadzula Paulo. Choncho analamula asilikali kuti apite akamuchotse pagululo nʼkubwera naye kumpanda wa asilikali.

11 Koma usiku wa tsiku lomwelo, Ambuye anaima pafupi ndi Paulo nʼkumuuza kuti: “Limba mtima.+ Chifukwa wandichitira umboni mokwanira ku Yerusalemu, ndipo ukandichitiranso umboni ku Roma.”+

12 Kutacha, Ayuda anakonza chiwembu nʼkulumbira pochita kudzitemberera kuti saadya kapena kumwa chilichonse mpaka atapha Paulo. 13 Panali amuna oposa 40 amene anakonza chiwembu chochita kulumbirirachi. 14 Anthuwa anapita kwa ansembe aakulu ndi akulu kukanena kuti: “Ife talumbira pochita kudzitemberera kuti sitidya chilichonse mpaka titapha Paulo. 15 Tsopano inuyo ndi Khoti Lalikulu la Ayuda, muuze mkulu wa asilikali kuti abweretse Paulo kwa inu ngati kuti mukufuna kumvetsa bwino nkhani yake. Koma asanafike ife tidzamupha.”

16 Koma mwana wamwamuna wa mchemwali wake wa Paulo anamva kuti anthuwo akonza zokamudikirira panjira, ndipo anapita kumpanda wa asilikali nʼkukamuuza Paulo zimenezi. 17 Choncho Paulo anaitana mmodzi wa atsogoleri a asilikali nʼkumuuza kuti: “Mʼtenge mnyamatayu upite naye kwa mkulu wa asilikali chifukwa ali ndi mawu oti akamuuze.” 18 Choncho anamutengadi nʼkupita naye kwa mkulu wa asilikali ndipo ananena kuti: “Paulo, mkaidi uja, anandiitana nʼkundiuza kuti ndimubweretse mnyamatayu. Akuti ali ndi mawu oti akuuzeni.” 19 Mkulu wa asilikaliyo anamugwira dzanja mnyamatayo nʼkupita naye pambali ndipo anamufunsa kuti: “Ukufuna kundiuza chiyani?” 20 Iye anati: “Ayuda agwirizana zoti akupempheni kuti mawa mupititse Paulo kubwalo la Khoti Lalikulu la Ayuda, ngati kuti akufuna kumvetsa bwino mlandu wake.+ 21 Koma musalole kuti akunyengerereni, chifukwa amuna oposa 40 akufuna kudzamudikirira panjira. Anthu amenewa alumbira mochita kudzitemberera kuti saadya kapena kumwa chilichonse mpaka atamupha.+ Moti panopa akonzeka, akungoyembekezera chilolezo chanu.” 22 Mkulu wa asilikaliyo anauza mnyamatayo kuti azipita atamulangiza kuti: “Usauze aliyense kuti wandifotokozera zimenezi.”

23 Ndiyeno anaitanitsa atsogoleri awiri a asilikali nʼkuwauza kuti: “Uzani asilikali 200 kuti akonzekere kuyenda ulendo wopita ku Kaisareya cha mʼma 9 koloko* usiku uno. Pakhalenso amuna 70 okwera pamahatchi* ndiponso asilikali 200 a mikondo. 24 Muwapatsenso mahatchi oti akwezepo Paulo kuti akafike kwa bwanamkubwa Felike ali wotetezeka.” 25 Ndiyeno iye analemba kalata yonena kuti:

26 “Ine Kalaudiyo Lusiya, ndikulembera inu Wolemekezeka Bwanamkubwa Felike: Landirani moni! 27 Munthu uyu anagwidwa ndi Ayuda ndipo anatsala pangʼono kumupha. Koma nthawi yomweyo ndinafika ndi gulu langa la asilikali nʼkumupulumutsa,+ chifukwa ndinamva kuti iyeyu ndi nzika ya Roma.+ 28 Ndiyeno pofuna kudziwa chimene anapalamula, ndinapita naye ku Khoti Lalikulu la Ayuda.+ 29 Kumeneko ndinapeza kuti akumuimba mlandu pa nkhani zokhudza Chilamulo chawo.+ Koma sanapezeke ndi mlandu uliwonse woyenera kuphedwa kapena kutsekeredwa mʼndende. 30 Komabe popeza ndadziwa chiwembu chimene amukonzera munthuyu,+ ndamutumiza kwa inu, ndipo ndalamula omuimba mlanduwo kuti adzanene mlandu wake pamaso panu.”

31 Choncho asilikaliwo anatenga Paulo+ usiku nʼkupita naye ku Antipatiri mogwirizana ndi zimene anawalamula. 32 Tsiku lotsatira anasiya amuna okwera pamahatchi aja kuti apitirire naye, koma iwo anabwerera kumpanda wa asilikali. 33 Amuna okwera pamahatchiwo anafika ku Kaisareya nʼkupereka kalata ija kwa bwanamkubwa ndipo anaperekanso Paulo. 34 Choncho bwanamkubwayo anawerenga kalatayo ndipo anafunsa chigawo chimene Paulo ankachokera. Anamva kuti ankachokera ku Kilikiya.+ 35 Ndiyeno anati: “Ndimvetsera mlandu wako wonse anthu okuimba mlanduwo akafika.”+ Ndipo analamula kuti amusunge mʼnyumba ya Mfumu Herode nʼkumamulondera.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena