Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 6
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Zimene Zili Mʼbuku la Deuteronomo

      • Muzikonda Yehova ndi mtima wanu wonse (1-9)

        • “Tamverani Aisiraeli inu” (4)

        • Makolo aziphunzitsa ana (6, 7)

      • Musaiwale Yehova (10-15)

      • Musamamuyese Yehova (16-19)

      • Mudzafotokozere mʼbadwo wotsatira (20-25)

Deuteronomo 6:2

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 18:19; De 4:9
  • +Miy 3:1, 2

Deuteronomo 6:4

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 5:7; Yes 42:8; Zek 14:9; Mko 12:29, 32; 1Ak 8:6

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda (Yophunzira),

    6/2016, ptsa. 18-22

    Nsanja ya Olonda,

    3/1/2012, tsa. 23

    12/15/1992, tsa. 29

    Kukambitsirana, ptsa. 392, 402

Deuteronomo 6:5

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 10:12; 11:13; 30:6; Mt 22:37
  • +Mko 12:30, 33; Lu 10:27

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    5/15/2007, ptsa. 15-16

    6/15/2005, tsa. 20

    10/1/1995, tsa. 13

Deuteronomo 6:6

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale, lesson 50

    Nsanja ya Olonda,

    4/1/2008, tsa. 14

    5/15/2007, ptsa. 15-16

    4/1/2006, ptsa. 8-9

    6/15/2005, tsa. 20

    4/1/2005, ptsa. 11-12

    6/1/1998, tsa. 20

    12/1/1996, tsa. 11

    7/1/1991, tsa. 26

    8/15/1988, tsa. 11

    Chinsinsi cha Banja, ptsa. 55-57, 58-59, 70-71

Deuteronomo 6:7

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “muziwaphunzitsa mobwerezabwereza kuti akhazikike.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 18:19; De 4:9; Miy 22:6; Aef 6:4
  • +De 11:19

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale, lesson 50

    Nsanja ya Olonda (Yophunzira),

    12/2019, tsa. 26

    Nsanja ya Olonda,

    8/15/2013, tsa. 16

    4/1/2008, tsa. 14

    9/1/2007, tsa. 22

    5/15/2007, ptsa. 15-16

    11/1/2006, ptsa. 4-6

    4/1/2006, ptsa. 8-9

    6/15/2005, ptsa. 20-21

    4/15/2005, ptsa. 6-7

    4/1/2005, ptsa. 11-12

    1/1/2005, tsa. 26

    6/15/2004, tsa. 5

    6/1/1998, ptsa. 20-22

    12/1/1996, tsa. 11

    5/1/1995, tsa. 10

    6/15/1989, tsa. 20

    Chinsinsi cha Banja, ptsa. 55-57, 58-59, 70-71

Deuteronomo 6:8

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “pakati pa maso anu.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 11:18

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    4/1/2005, tsa. 13

    9/15/2004, tsa. 26

    7/15/1995, tsa. 29

    5/1/1995, ptsa. 11-12

    8/15/1988, tsa. 11

Deuteronomo 6:9

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    4/1/2005, tsa. 13

    7/15/1995, tsa. 29

    5/1/1995, ptsa. 11-12

Deuteronomo 6:10

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 15:18
  • +Yos 24:13; Sl 105:44

Deuteronomo 6:11

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 8:10

Deuteronomo 6:12

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Owe 3:7

Deuteronomo 6:13

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 10:12; 13:4
  • +Lu 4:8
  • +Yer 12:16

Deuteronomo 6:14

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 34:14

Deuteronomo 6:15

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 20:5; De 4:24
  • +Eks 32:9, 10; Nu 25:3; De 11:16, 17; Owe 2:14
  • +2Mf 17:18

Deuteronomo 6:16

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mt 4:7; Lu 4:12; 1Ak 10:9
  • +Eks 17:2, 7; Sl 95:8, 9; Ahe 3:8, 9

Deuteronomo 6:18

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 15:18

Deuteronomo 6:19

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 23:30

Deuteronomo 6:22

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 7:3
  • +De 4:34

Deuteronomo 6:23

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 13:5; De 1:8

Deuteronomo 6:24

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Sl 111:10; Miy 14:27
  • +Le 18:5; De 4:1; Aga 3:12

Deuteronomo 6:25

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “pamaso pa.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mla 12:13; Aro 10:5

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Deut. 6:2Ge 18:19; De 4:9
Deut. 6:2Miy 3:1, 2
Deut. 6:4De 5:7; Yes 42:8; Zek 14:9; Mko 12:29, 32; 1Ak 8:6
Deut. 6:5De 10:12; 11:13; 30:6; Mt 22:37
Deut. 6:5Mko 12:30, 33; Lu 10:27
Deut. 6:7Ge 18:19; De 4:9; Miy 22:6; Aef 6:4
Deut. 6:7De 11:19
Deut. 6:8De 11:18
Deut. 6:10Ge 15:18
Deut. 6:10Yos 24:13; Sl 105:44
Deut. 6:11De 8:10
Deut. 6:12Owe 3:7
Deut. 6:13De 10:12; 13:4
Deut. 6:13Lu 4:8
Deut. 6:13Yer 12:16
Deut. 6:14Eks 34:14
Deut. 6:15Eks 20:5; De 4:24
Deut. 6:15Eks 32:9, 10; Nu 25:3; De 11:16, 17; Owe 2:14
Deut. 6:152Mf 17:18
Deut. 6:16Mt 4:7; Lu 4:12; 1Ak 10:9
Deut. 6:16Eks 17:2, 7; Sl 95:8, 9; Ahe 3:8, 9
Deut. 6:18Ge 15:18
Deut. 6:19Eks 23:30
Deut. 6:22Eks 7:3
Deut. 6:22De 4:34
Deut. 6:23Eks 13:5; De 1:8
Deut. 6:24Sl 111:10; Miy 14:27
Deut. 6:24Le 18:5; De 4:1; Aga 3:12
Deut. 6:25Mla 12:13; Aro 10:5
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Deuteronomo 6:1-25

Deuteronomo

6 “Tsopano amenewa ndi malamulo, malangizo ndi zigamulo zimene Yehova Mulungu wanu wandipatsa kuti ndikuphunzitseni, kuti muzikazitsatira mukawoloka mtsinje wa Yorodano nʼkupita mʼdziko limene mukukalitenga kuti likhale lanu, 2 kuti muziopa Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira malangizo ake komanso malamulo ake amene ndikukuuzani, inuyo, ana anu ndi zidzukulu zanu,+ masiku onse a moyo wanu, nʼcholinga choti mukhale ndi moyo nthawi yaitali.+ 3 Ndipo inu Aisiraeli, muzimvetsera ndi kutsatira malangizo ndi malamulo akewo mosamala, kuti zinthu zikuyendereni bwino komanso kuti muchuluke kwambiri mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi, mogwirizana ndi zimene Yehova, Mulungu wa makolo anu anakulonjezani.

4 Tamverani, Aisiraeli inu: Yehova Mulungu wathu ndi Yehova mmodzi.+ 5 Muzikonda Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, moyo wanu wonse+ ndi mphamvu zanu zonse.+ 6 Mawu awa amene ndikukulamulani lerowa azikhala pamtima panu, 7 ndipo muziwakhomereza* mumtima mwa ana anu.+ Muzilankhula nawo mawuwo mukakhala pansi mʼnyumba mwanu, mukamayenda pamsewu, mukamagona komanso mukadzuka.+ 8 Muwamange padzanja lanu kuti muziwakumbukira, ndipo azikhala ngati chomanga pachipumi panu.*+ 9 Muwalembe pamafelemu a nyumba zanu komanso pamageti a mzinda wanu.

10 Ndiyeno Yehova Mulungu wanu akadzakulowetsani mʼdziko limene analumbira kwa makolo anu Abulahamu, Isaki ndi Yakobo kuti adzakupatsani,+ dziko lokhala ndi mizinda ikuluikulu yabwino imene simunamange ndinu,+ 11 yokhalanso ndi nyumba zodzaza ndi zinthu zosiyanasiyana zabwino zimene simunagwirire ntchito, zitsime zimene simunakumbe ndinu komanso minda ya mpesa ndi mitengo ya maolivi imene simunadzale ndinu, ndiye mukakadya nʼkukhuta,+ 12 mukasamale kuti musakaiwale Yehova+ amene anakutulutsani mʼdziko la Iguputo, mʼnyumba yaukapolo. 13 Muziopa Yehova Mulungu wanu+ nʼkumamutumikira,+ ndipo muzilumbira pa dzina lake.+ 14 Musatsatire milungu ina, milungu iliyonse ya anthu amene akuzungulirani,+ 15 chifukwa Yehova Mulungu wanu amene ali pakati panu ndi Mulungu amene amafuna kuti anthu azidzipereka kwa iye yekha basi.+ Mukatsatira milungu ina, mkwiyo wa Yehova Mulungu wanu udzakuyakirani+ ndipo adzakufafanizani padziko lapansi.+

16 Yehova Mulungu wanu musamamuyese+ ngati mmene munamuyesera ku Masa.+ 17 Muzionetsetsa kuti mukusunga malamulo a Yehova Mulungu wanu, zikumbutso zake ndi malangizo ake amene wakulamulani kuti muziwatsatira. 18 Muzichita zoyenera ndi zabwino pamaso pa Yehova kuti zikuyendereni bwino komanso kuti mukalowe mʼdziko labwino limene Yehova analumbira kwa makolo anu, nʼkulitenga kuti likhale lanu,+ 19 pothamangitsa adani anu onse mogwirizana ndi zimene Yehova analonjeza.+

20 Mʼtsogolo mwana wanu akadzakufunsani kuti, ‘Kodi zikumbutso, malangizo ndi zigamulo zimene Yehova Mulungu wathu anakupatsani zimatanthauza chiyani?’ 21 mwana wanuyo mudzamuyankhe kuti, ‘Tinali akapolo a Farao ku Iguputo, koma Yehova anatitulutsa ku Iguputoko ndi dzanja lamphamvu. 22 Choncho Yehova anapitiriza kuchita zizindikiro ndi zodabwitsa zazikulu ndiponso zowononga mu Iguputo monse,+ kwa Farao ndi kwa anthu onse amʼnyumba mwake, ife tikuona.+ 23 Ndipo anatitulutsa kumeneko kuti atibweretse kuno kudzatipatsa dziko limene analumbira kwa makolo athu.+ 24 Ndiyeno Yehova anatilamula kuti tizitsatira malangizo onsewa komanso kuti tiziopa Yehova Mulungu wathu kuti zinthu zizitiyendera bwino nthawi zonse,+ komanso kuti tikhale ndi moyo+ ngati mmene zilili lero. 25 Ndipo tikamatsatira malamulo onsewa mosamala kwambiri pomvera* Yehova Mulungu wathu mogwirizana ndi zimene anatilamula, ndiye kuti tikuchita chilungamo pamaso pake.’”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena