Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • nwt Obadiah 1-21
  • Obadiya

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Obadiya
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Obadiya

OBADIYA

1 Awa ndi masomphenya a Obadiya:*

Zimene Yehova Ambuye Wamkulu Koposa akunena zokhudza Edomu+ ndi izi:

“Ife tamva uthenga wochokera kwa Yehova,

Ndipo nthumwi yatumidwa kwa anthu amitundu ina kukanena kuti:

‘Konzekani! Tiyeni tikamenyane naye.’”+

 2 “Taona! Ndakuchititsa kukhala wosafunika pakati pa mitundu ina,

Ndipo ikukuona kuti ndiwe wonyozeka kwambiri.+

 3 Mtima wako wodzikuza wakupusitsa,+

Iwe amene ukukhala mʼmalo obisika amʼthanthwe,

Uli pamwamba pa phiri nʼkumanena mumtima mwako kuti,

‘Ndani angandigwetsere pansi?’

 4 Ngakhale utamakhala mʼmwamba* ngati chiwombankhanga,

Kapena utamanga chisa chako pakati pa nyenyezi,

Ine ndidzakugwetsapo pamenepo,” akutero Yehova.

 5 “Akuba atabwera kwa iwe, kapena mbava zitabwera usiku,

Kodi sangabe zokhazo zimene akufuna?

(Koma ndiye udzawonongedwatu!)*

Kapena okolola mphesa atabwera kwa iwe,

Kodi sangasiyeko zina zoti munthu nʼkukunkha?+

 6 Koma Esau ndiye wafufuzidwatu!

Anthu asakasaka chuma chake chonse chobisika nʼkuchitenga.

 7 Anthu amene unachita nawo mgwirizano* akuthamangitsira kumalire.

Onsewo akupusitsa.

Anthu amene unkakhala nawo mwamtendere akugonjetsa.

Anthu amene ukudya nawo limodzi adzakutchera ukonde,

Koma iwe sudzazindikira.”

 8 Yehova akuti: “Kodi pa tsiku limenelo,

Sindidzawononga anthu anzeru mu Edomu,+

Komanso anthu ozindikira mʼdera lamapiri la Esau?

 9 Iwe Temani,+ asilikali ako adzachita mantha,+

Chifukwa aliyense mʼdera lamapiri la Esau adzaphedwa.+

10 Popeza unachitira nkhanza mʼbale wako Yakobo,+

Udzachititsidwa manyazi kwambiri.+

Udzaphedwa ndipo sudzakhalaponso mpaka kalekale.+

11 Pa tsiku limene unangoima nʼkumaonerera,

Pa tsiku limene adani* anagwira gulu la asilikali a mʼbale wako nʼkupita nawo ku ukapolo,+

Ndiponso pamene anthu akudziko lina analowa mumzinda* wake nʼkuchita maere+ pa Yerusalemu,

Iwe unali ngati mmodzi wa adaniwo.

12 Iwe sumayenera kunyadira pa tsiku limene mʼbale wako anakumana ndi tsoka,+

Sumayenera kusangalala pa tsiku limene anthu a ku Yuda ankawonongedwa,+

Sumayeneranso kulankhula modzitama pa tsiku limene ankazunzika.

13 Iwe sumayenera kulowa mumzinda* wa anthu anga pa tsiku limene anakumana ndi tsoka.+

Sumayenera kunyadira pamene mʼbale wako ankavutika pa tsiku limene anakumana ndi tsoka.

Ndipo sumayeneranso kutenga chuma chake pa tsiku limene anakumana ndi tsoka.+

14 Iwe sumayenera kuima panjira kuti uzipha anthu ake amene akuthawa.+

Sumayeneranso kugwira anthu ake amene apulumuka nʼkuwapereka kwa adani awo pa tsiku limene ankazunzika.+

15 Tsiku la Yehova limene adzalange mitundu yonse ya anthu lili pafupi.+

Zimene wachitira mʼbale wako, iwenso adzakuchitira zomwezo.+

Zimene unachitira anthu ena zidzakubwerera pamutu pako.

16 Mmene wamwera vinyo paphiri langa loyera,

Ndi mmenenso mitundu ina yonse ya anthu izidzamwera mkwiyo wanga nthawi zonse.+

Iwo adzamwa ndi kugugudiza mkwiyo wanga,

Ndipo zidzakhala ngati sanakhalepo nʼkomwe.

17 Anthu onse opulumuka adzakhala paphiri la Ziyoni+

Ndipo phiri limeneli lidzakhala loyera.+

Anthu a mʼbanja la Yakobo adzatenganso zinthu zimene zinali zawo.+

18 A mʼbanja la Yakobo adzakhala ngati moto,

A mʼbanja la Yosefe adzakhala ngati malawi a moto,

Ndipo a mʼbanja la Esau adzakhala ngati mapesi.

Moto wawo udzayatsa ndi kunyeketsa mapesiwo,

Ndipo palibe aliyense wa mʼbanja la Esau amene adzapulumuke,+

Chifukwa Yehova ndi amene wanena.

19 Iwo adzatenga dera la Negebu ndi dera lamapiri la Esau,+

Komanso dera la Sefela ndi dera la Afilisiti.+

Adzatenganso madera a Efuraimu ndi Samariya,+

Ndipo Benjamini adzatenga dera la Giliyadi.

20 Anthu amene anatengedwa pamalo okwera omenyerapo nkhondowa nʼkupita nawo kudziko lina,+

Amene ndi Aisiraeli, adzatenga dziko la Akanani mpaka kukafika ku Zarefati.+

Anthu amene anatengedwa kuchokera ku Yerusalemu, amene anali ku Sefaradi, adzatenga mizinda ya Negebu.+

21 Opulumutsa adzakwera paphiri la Ziyoni

Kuti aweruze dera lamapiri la Esau,+

Ndipo Yehova adzakhala Mfumu.”+

Kutanthauza “Mtumiki wa Yehova.”

Mabaibulo ena amati, “utaulukira mʼmwamba.”

Mabaibulo ena amati, “Kodi angawononge zambiri bwanji?”

Kapena kuti, “pangano.”

Mʼchilankhulo choyambirira, “anthu achilendo.”

Mʼchilankhulo choyambirira, “pageti.”

Mʼchilankhulo choyambirira, “pageti.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena