Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w91 1/1 tsamba 30
  • Iye Anapeza Katrakiti Panjanji

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Iye Anapeza Katrakiti Panjanji
  • Nsanja ya Olonda—1991
Nsanja ya Olonda—1991
w91 1/1 tsamba 30

Iye Anapeza Katrakiti Panjanji

MUNALI m’chaka cha 1921. M’mapiri a Transvaal, dera la South Africa, gulu la amuna okonza njanji ankagwira ntchito panjanji yasitima. Kapitawo wa gululo, wolankhula Chiafrikaner wotchedwa Christiaan Venter, anawona kachidutswa kapepala kosomekedwa kunsi kwa njanji. Iko kanali katrakiti kofalitsidwa ndi Watch Tower Bible and Tract Society.

Pamene analamulira amuna ake kuima, Christiaan anakaŵerenga ndi chikondwerero chachikulu. Iye anathamangira kukakomana ndi mkamwini wake, Abraham Celliers, namufotokozera mokondwera kuti: “Abraham, lero ndachipeza chowonadi!”

Mwamsanga pambuyo pake, iwo analembera afalitsi a katrakitiko kuti amve zambiri. Powayankha, nthambi ya ku South Africa ya Watch Tower Society inaŵatumizira mabuku owonjezereka a Baibulo. Amuna aŵiriwa anaŵaphunzirira pamodzi pa nthaŵi ya kupuma kwawo ndiusiku kwambiri. Mofulumira anayamba kugawana chowonadicho ndi mabwenzi ndi alendo.

Pomalizira pake, onse aŵiri Christiaan ndi Abraham anakhala Mboni zobatizidwa za Yehova. Monga chotulukapo cha changu chawo ndi kukhulupirika, anthu ambiri a ku South Africa anathandizidwa kudziŵa chowonadi. Kuwonjezera apa, mbadwa zawo zoposa zana limodzi ziri Mboni za Yehova zokangalika lerolino! Mmodzi wa iwo akutumikira pamalikulu a Mboni za Yehova m’Brooklyn, New York, ndipo wina ali pa ofesi ya Watch Tower Society mu South Africa.

Lerolino, zaka 70 pambuyo pake, matrakiti a Baibulo akupitirizabe kuchita mbali yaikulu m’kufalitsa uthenga Waufumu.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena