Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w96 3/1 tsamba 32
  • Ŵalitsani Kuunika Kwanu!

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Ŵalitsani Kuunika Kwanu!
  • Nsanja ya Olonda—1996
Nsanja ya Olonda—1996
w96 3/1 tsamba 32

Ŵalitsani Kuunika Kwanu!

POMALIZIRA pake nthaŵi inafika yakuti mwamuna wokalambayo aone Mesiya wolonjezedwa! Mwa vumbulutso la Mulungu Simeoni anadziŵa kuti ‘sadzaona imfa, kufikira adzaona Kristu wake wa Yehova.’ (Luka 2:26) Koma zinali zokondweretsa chotani nanga pamene Simeoni analoŵa m’kachisi ndipo Mariya ndi Yosefe naika khandalo Yesu m’manja mwake! Anatamanda Mulungu, akumati: “Tsopano, Ambuye, . . . lolani ine, kapolo wanu, ndichoke mumtendere; chifukwa maso anga adaona chipulumutso chanu, . . . kuunika kukhale chivumbulutso cha kwa anthu a mitundu, ndi ulemerero wa anthu anu Israyeli.”​—Luka 2:27-32; yerekezerani ndi Yesaya 42:1-6.

Yesu, kuyambira pa ubatizo wake pausinkhu wa zaka 30 kufikira pa imfa yake, anakhala “kuunika” kwa dziko. M’njira zotani? Iye anatulutsa kuunika kwauzimu mwa kulalikira za Ufumu wa Mulungu ndi zifuno Zake. Anavumbulanso ziphunzitso zonyenga zachipembedzo ndi kudziŵikitsa poyera ntchito zimene zinali zamdima. (Mateyu 15:3-9; Agalatiya 5:19-21) Chotero, Yesu anatha kunena molondola kuti: “Ine ndine kuunika kwa dziko lapansi.”​—Yohane 8:12.

Yesu anafa m’chaka cha 33 C.E. Kodi panthaŵiyo kuunika kunazima? Kutalitali! Akali padziko lapansi, Yesu anauza ophunzira ake kuti: “Muŵalitse inu kuunika kwanu pamaso pa anthu.” (Mateyu 5:16) Moyenerera, imfa ya Yesu itachitika ophunzira ake anaŵalitsa kuunika kwawo.

Potsanzira Yesu, Akristu lerolino amatulutsa kuunika kwa Yehova mwa kuchita ntchito yolalikira. ‘Amayenda monga ana a kuunika,’ akumadzisonyeza kukhala zitsanzo zapadera pamoyo wachikristu.​—Aefeso 5:8.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena