Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w98 9/15 tsamba 32
  • Nkhondo Yomwe Inawononga Zaka za Zana la 19

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Nkhondo Yomwe Inawononga Zaka za Zana la 19
  • Nsanja ya Olonda—1998
Nsanja ya Olonda—1998
w98 9/15 tsamba 32

Nkhondo Yomwe Inawononga Zaka za Zana la 19

1914

POKUMBUKIRA za zaka chikwi zatsopano, Charley Reese, wolemba nyuzipepala ya The Orlando Sentinel, analemba kuti: “Nkhondo ya mu 1914-18 yomwe inawononga zaka za zana la 19 sinathebe.” Kodi iye anatanthauzanji? Iye anafotokoza kuti: “Mbiri sigonera. Zaka za zana la 19​—zofotokozedwa mwa zikhulupiriro zake, zitsimikizo, malingaliro ndi makhalidwe abwino​—sizinathe pa Jan. 1, 1901. Zinatha mu 1914. Nthaŵi imeneyo mpamenenso zaka za zana la 20 zinayamba, zofotokozedwanso mofananamo. . . .

“Mwachionekere, mikangano yonse imene yachitika ife tilipo ndi moyo inachokera kunkhondo imeneyo. Pafupifupi zonse za maphunziro ndi zikhalidwe zimene takhala nazo zinayambika ndi nkhondo imeneyo. . . .

“Ndiganiza kuti nkhondoyo inasokoneza zinthu chifukwa chakuti inathetsa chikhulupiriro chimene anthu anali nacho chakuti iwo angalamulire zimene zidzawachitikira mtsogolo. . . . Nkhondoyo inachititsa anthu kukana chikhulupiriro chimenecho. Palibe gulu lililonse mwa magulu omenyanawo limene linaganizapo kuti zidzakhala mmene zinakhalira. Inawononga ufumu wa Britain ndi ufumu wa France. Inapha anthu ofunika kwambiri a mbadwowo ku Britain, France ndi Germany. . . . M’nthaŵi yochepa chabe, inapha anthu 11 miliyoni.”

Kwazaka zoposa 120, Mboni za Yehova zakhala zikufotokoza kuti 1914 inali mapeto a zimene Yesu anazitcha “nthaŵi zawo za anthu akunja.” (Luka 21:24) M’chaka chimenecho, Yesu Kristu woukitsidwa ndi wokwezekayo anaikidwa monga Mfumu ya Ufumu wakumwamba. Mwa Ufumu umenewo, Yehova Mulungu adzachotseratu mavuto onse omwe akhala akuchitika m’zaka za zana lino.​—Salmo 37:10, 11; Mlaliki 8:9; Chivumbulutso 21:3, 4.

[Mawu a Chithunzi patsamba 32]

Chithunzi cha U.S. National Archives

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena