Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w00 1/15 tsamba 32
  • Chaka Chabwino Kwambiri Kugaŵira Mabaibulo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Chaka Chabwino Kwambiri Kugaŵira Mabaibulo
  • Nsanja ya Olonda—2000
Nsanja ya Olonda—2000
w00 1/15 tsamba 32

Chaka Chabwino Kwambiri Kugaŵira Mabaibulo

ANTHU ambiri lerolino kuposa kale, ali ndi Baibulo. Izi n’zimene lipoti la United Bible Societies likunena, popeza mabaibulo amene anagaŵira mu 1998 anaposa amene anagaŵiridwa mu 1997 ndi 500,000. Onse pamodzi, mabaibulo athunthu kapena mbali yake amene anagaŵiridwa padziko lonse anali 585,000,000. “Izi n’zolimbikitsa,” likutero lipotilo. “Lerolino anthu ambiri ali ndi Mawu a Mulungu.”

Ndithudi, pali kusiyana pakati pa kukhala ndi Baibulo ndi kuliŵerenga. Mwachitsanzo, pakufufuza kwina anapeza kuti kuposa 90 peresenti ya nzika za ku United States zili ndi Baibulo, ndipo chiŵerengero chofananacho cha anthu chimakhulupirira kuti m’Baibulo ndimo muli ziphunzitso za makhalidwe abwino. Komabe, 59 peresenti okha n’ngomwe anati amapeza malangizo m’Baibulo. Ndipo 29 peresenti anavomereza kuti “salidziŵa kwenikweni” kapena “salidziŵa n’komwe” Baibulo.

Mboni za Yehova sizimangosindikiza ndi kugaŵira mabaibulo komanso zimapereka kwa anthu maphunziro a Baibulo aulere apanyumba m’mayiko 230. Tsopano mamiliyoni ambiri padziko lonse akupindula ndi pologalamu yophunzitsa Baibulo imeneyi. Akuthandizidwa kugonjetsa mavuto amene amakumana nawo lerolino, ndipo amaphunzira zimene Baibulo limanena pa za m’tsogolo mwabwino mu Ufumu wa Mulungu.​—Yesaya 48:17, 18; Mateyu 6:9, 10.

[Zithunzi patsamba 32]

Maphunziro a Baibulo apanyumba (kuyambira pamwamba kumanzere kumka kumanja) Bolivia, Ghana, Sri Lanka, ndi England

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena