Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w01 10/1 tsamba 19
  • Kulalikira Anthu Ovuta Kuwapeza

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kulalikira Anthu Ovuta Kuwapeza
  • Nsanja ya Olonda—2001
  • Nkhani Yofanana
  • Mboni Za Yehova—Gulu la Dzinalo
    Nsanja ya Olonda—1992
  • Kutsogoza Ophunzira ku Gulu la Dzina lathu
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1997
  • Zida Zimene Zimaphunzitsa, Kusonkhezera, ndi Kulimbikitsa
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2000
  • Kuchititsa Maphunziro a Baibulo Opita Patsogolo Gawo 8
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2001
w01 10/1 tsamba 19

Olengeza Ufumu Akusimba

Kulalikira Anthu Ovuta Kuwapeza

MBONI ZA YEHOVA zimayesetsa kulalikira uthenga wa Ufumu kwa aliyense amene zingakumane naye. Nthaŵi zina, kulalikira anthu amene kaŵirikaŵiri sapezeka pa nyumba kumafunika khama lapadera. (Marko 13:10) Mpainiya wina wapadera m’dziko lina ku South America akusimba zomwe anachita pankhaniyi.

“Tsiku lina ndinamva kuti wolamulira wa dzikolo adzabwera kudzayendera dera lomwe ine ndi mkazi wanga tinali kulalikira. Popeza kuti iye mwachionekere anali m’gulu la anthu amene kaŵirikaŵiri sapezeka pa nyumba, ndinamulembera kalata ndipo m’kalatayo ndinaikamo mabuku ofotokoza Baibulo angapo, kuphatikizapo bulosha lakuti Kodi Mulungu Amafunanji kwa Ife? komanso buku lakuti Mankind’s Search for God ndi Chidziŵitso Chotsogolera ku Moyo Wosatha. M’kalatayo ndinafotokoza cholinga cha mabuku ameneŵa lililonse palokha.

“Popeza kuti ndinkafuna kudziŵa maganizo ake pa mabuku ameneŵa, ndinapempha kuti ndikaonane naye. Patapita milungu ingapo, anandilola ndipo popita ndinatenga vidiyo yakuti Jehovah’s Witnesses​—The Organization Behind the Name. Ndinacheza naye kwa maola aŵiri. Titaonerera limodzi vidiyoyo, ndinam’funsa maganizo ake pa vidiyoyo. Anayankha amvekere: ‘Palibenso gulu ngati lanuli padziko lapansi. Ndikulakalaka ndikanakhala ndi anthu ngati inu amene akanandithandiza kukwaniritsa zolinga za boma langa!’ Kenako anandifunsa ngati ndinapitako kulikulu la dziko lonse la gulu lathu. Ndinamuuza kuti ngakhale kuti kuyambira ndili ndi zaka 14 ndicho chakhala cholinga changa, sindinapezebe mwayi wokaona likulu lathu la dziko lonse ku Brooklyn, New York. Chinalitu chimodzi mwa zolinga zovuta kuzikwaniritsa. Anandiyang’anitsitsa mwachidwi kwakanthaŵi ndithu. Kenako ananena kuti akufuna kuti ndipeze mwayi umenewo. Anatikonzera makalata otilola mwalamulo ndipo anatipatsa mphatso ya tikiti ya ndege!

“Wolamulirayo tsopano amalandira magazini a Nsanja ya Olonda ndi Galamukani! nthaŵi zonse. Tikukhulupirira kuti mwina posachedwapa tiyamba kuphunzira naye Baibulo.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena