Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w02 3/15 tsamba 32
  • Chochitika Chofunika Koposa M’mbiri

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Chochitika Chofunika Koposa M’mbiri
  • Nsanja ya Olonda—2002
Nsanja ya Olonda—2002
w02 3/15 tsamba 32

Chochitika Chofunika Koposa M’mbiri

CHINALI imfa ya Yesu Kristu. N’chifukwa chiyani inali yofunika kwambiri? Pali zifukwa zingapo.

Kukhulupirika kwa Yesu mpaka imfa kunasonyeza kuti munthu atha kupitirizabe kukhala wokhulupirika kwa Mulungu.

Imfa ya Kristu inapatsa mwayi anthu ena kuti akakhale olamulira limodzi naye kumwamba. Inatsegulanso njira kwa anthu ena ambiri kuti adzakhale ndi moyo wosatha m’dziko lapansi la paradaiso.

Yesu pausiku woti aphedwa mawa, anagwiritsa ntchito mkate wopanda zofufumitsa ndi vinyo wofiira monga zizindikiro zoimira nsembe yachikondi ya thupi lake. Ndipo iye anauza ophunzira ake kuti: “Chitani ichi chikumbukiro changa.” (Luka 22:19) Kodi mudzakumbukira nawo chochitika chofunika kwambirichi?

Mboni za Yehova zikukuitanani kuti mudzakhale nazo pa mwambo wa Chikumbutso cha imfa ya Yesu. Chaka chino mwambo umenewu udzachitika Lachinayi, March 28, dzuŵa litaloŵa. Mutha kudzafika ku Nyumba ya Ufumu yomwe ili kufupi ndi kwanu. Chonde funsani Mboni za Yehova zakwanuko kuti zikuuzeni nthaŵi yeniyeni ndi malo ake.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena