Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w07 1/15 tsamba 3
  • Mwamuna ndi Mkazi Anapangidwa Kuti Azithandizana

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mwamuna ndi Mkazi Anapangidwa Kuti Azithandizana
  • Nsanja ya Olonda—2007
  • Nkhani Yofanana
  • Mwamuna ndi Mkazi Oyamba
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Mulungu Analenga Anthu Awiri Oyamba
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Ziyembekezo Zazikulu za Anthu M’paradaiso ya Chisangalalo
    Nsanja ya Olonda—1989
  • Mbali ya Mkazi m’Malemba
    Nsanja ya Olonda—1991
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2007
w07 1/15 tsamba 3

Mwamuna ndi Mkazi Anapangidwa Kuti Azithandizana

KUYAMBIRA kale mwamuna ndi mkazi akhala akulakalaka kukhala limodzi. Mulungu ndiye anayambitsa zimenezi. Yehova anaona kuti sikunali kwabwino kuti mwamuna woyamba, Adamu, akhale yekha. Choncho Mulungu anam’pangira “wom’thangatira iye.”

Yehova anagonetsa Adamu tulo tatikulu, kenako anatenga nthiti yake imodzi ndipo “anaipanga mkazi, ndipo ananka naye kwa Adamu.” Iye anasangalala kwambiri ataona cholengedwa cha Mulungu chokongola chimenechi moti ananena kuti: “Uyu tsopano ndiye fupa la mafupa anga, ndi mnofu wa mnofu wanga.” Mkazi wangwiro ameneyu dzina lake linali Hava ndipo chifukwa cha makhalidwe ake achikazi, anali wokondedwa kwambiri. Adamu analinso wangwiro ndipo monga mwamuna anali wofunika kumulemekeza. Awiriwa anapangidwa kuti azithandizana. Baibulo limanena kuti: “Chifukwa chotero mwamuna adzasiya atate wake ndi amake nadzadziphatika kwa mkazi wake: ndipo adzakhala thupi limodzi.”​—Genesis 2:18-24.

Koma, masiku ano, mabanja akutha, ndipo mgwirizano wa mwamuna ndi mkazi nthawi zambiri umakhala wankhanza ndipo onse amachita zinthu modzikonda. Mtima wampikisano wachititsa kuti mwamuna ndi mkazi asamagwirizane. Zonsezi n’zosemphana ndi cholinga cha Mulungu chokhudza mwamuna ndi mkazi. Mwamuna anapangidwa kuti akwaniritse udindo wofunika kwambiri pa dziko lapansi. Mkazi anapangidwa kuti akhale ndi udindo wapadera ndi wolemekezeka wothandiza mwamuna wake. Onse anapangidwa kuti azigwira ntchito limodzi mogwirizana. Kuyambira chiyambi cha anthu, amuna ndi akazi omvera Mulungu akhala akuyesayesa mokhulupirika kukwaniritsa udindo womwe Yehova anawapatsa, ndipo kuchita zimenezi kwawathandiza kukhala achimwemwe ndi okhutira pa moyo wawo. Kodi udindo umenewu ndi wotani ndipo tingaukwaniritse motani?

[Chithunzi patsamba 3]

Mwamuna ndi mkazi anapangidwa kuti akhale ndi udindo wolemekezeka m’dongosolo la Mulungu

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena