Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w07 11/1 tsamba 3
  • Kudzichepetsa Sikophweka

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kudzichepetsa Sikophweka
  • Nsanja ya Olonda—2007
  • Nkhani Yofanana
  • Khalani Odzichepetsadi
    Nsanja ya Olonda—2005
  • Kodi Nkuvaliranji Kudzichepetsa?
    Nsanja ya Olonda—1991
  • Yehova Amaona Kuti Atumiki Ake Odzichepetsa Ndi Amtengo Wapatali
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2019
  • Zitsanzo za Kudzichepetsa Zoyenera Kutsanziridwa
    Nsanja ya Olonda—1993
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2007
w07 11/1 tsamba 3

Kudzichepetsa Sikophweka

PALI anthu ambiri amene amaona kuti khalidwe lodzichepetsa n’lachikale. Anthu ambiri aulemu wawo ndiponso omwe amaoneka kuti zinthu zikuwayendera kwambiri, amakhala odzitama, onyada, komanso ongoganizira zawo zokha basi. Pali anthu ambiri amene amakhumbira moyo wa anthu olemera ndi otchuka, koma osati wa anthu odzichepetsa ndi ofatsa. Nthawi zambiri, m’malo modzichepetsa, anthu olemerawa amadzitama, n’kumanena kuti chuma chawo chonsecho anachita kuchivutikira okha.

Wofufuza wina wa ku Canada anati m’dzikolo mwabweranso khalidwe lina lomangoganizira zako zokha basi. Palinso anthu ena amene akuona kuti anthu ambiri padzikoli amangokhalira kusangalala ndi kuchita zinthu mosaganizira kaye bwinobwino. Iwo amanena kuti anthu ambiri masiku ano akungoganizira zawo zokha basi. N’chifukwa chake masiku ano kudzichepetsa sikukuoneka ngati khalidwe labwino.

Komabe anthu ambiri angavomereze mfundo yakuti ndi bwino kuti anthu ena azikhala odzichepetsa, chifukwa choti anthu odzichepetsa savuta kuchita nawo zinthu. Komabe m’dziko lokonda kupikisanali, anthu ena sadzichepetsa poopa kuti akatero, anthu ayamba kuwaona kuti ndi ofooka.

Baibulo, lomwe ndi Mawu a Mulungu, linalosera kuti m’nthawi yathu ino anthu adzakhala “odzimva, odzikweza.” (2 Timoteyo 3:1, 2) Kodi mukuona kuti ulosi umenewu ukukwaniritsidwa? Nanga kodi mumaona kuti kukhala wodzichepetsa kuli ndi ubwino uliwonse? Kapena mumaganiza kuti anthu amaona kuti munthu wodzichepetsa ndi wofooka, wosavuta kumudyera masuku pamutu?

Baibulo limapereka zifukwa zomveka zosonyeza kuti khalidwe lodzichepetsa n’lofunika kwambiri. Limatithandiza kumvetsa bwino khalidweli ndi ubwino wokhala nalo, ndipo limasonyeza kuti kudzichepetsa kwenikweni si kufooka kapena mantha ayi. Nkhani yotsatirayi ifotokoza zifukwa zake.

[Chithunzi patsamba 3]

Kodi tiyenera kumva bwanji tikachita zinthu zinazake zotamandika?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena