Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w07 11/15 tsamba 32
  • “Chonde Landirani Kamphatso Kangaka”

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • “Chonde Landirani Kamphatso Kangaka”
  • Nsanja ya Olonda—2007
Nsanja ya Olonda—2007
w07 11/15 tsamba 32

“Chonde Landirani Kamphatso Kangaka”

MAWU amenewa analembedwa m’kalata imene ofesi ya nthambi ya Mboni za Yehova ku Russia inalandira, limodzi ndi bokosi lalikulu la masokosi.

Amene anatumiza mphatsoyi ndi mayi wina wazaka 67 dzina lake Alla. Iye ndi wa Mboni za Yehova ndipo ali mu mpingo wina kummawa kwa dziko la Russia. Alla wakhala akutumikira Yehova kwazaka zoposa 10. Iye wakhala akulalikira mwakhama uthenga wabwino wa Ufumu. Koma mwadzidzidzi anadwala matenda amene anapha ziwalo zake zina. Chifukwa cha chikondi, Alla anachita zinthu zofanana ndi zimene Dolika, mkazi wachikhristu wa m’nthawi ya atumwi, ankachita. Iye ankapangira Akhristu anzake zovala.​—Machitidwe 9:36, 39.

M’kalatayo, Alla analemba kuti: “Miyendo yanga sigwira ntchito, koma manja anga ndi abwinobwino. Choncho ndimalalikira kudzera m’makalata.” Iye anapitiriza kuti: “Ndinaganiza kuti popeza manja anga akugwirabe ntchito ndi bwino kuti ndiluke masokosi. Ndikufuna kuti masokosi amenewa aperekedwe kwa abale ndi alongo amene akukagwira ntchito yomanga Nyumba za Ufumu m’madera ozizira monga kummawa kwa dziko lino ndiponso ku Siberia.”

Ponena za otsatira ake enieni, Yesu Khristu anati: “Mwa ichi onse adzadziwa kuti ndinu ophunzira anga, ngati mukondana wina ndi mnzake.” (Yohane 13:35) Chikondi ngati chimene Alla anasonyeza ndi chizindikiro cha ophunzira enieni a Yesu.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena