Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w13 6/1 tsamba 16
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Nsanja ya Olonda—2013
  • Nkhani Yofanana
  • Mtendere Weniweni—Kodi Udzachokera Kuti?
    Nsanja ya Olonda—1997
  • Kodi Adzatsogolera Anthu ku Mtendere Ndani?
    Nsanja ya Olonda​—1990
  • Lolani “Mtendere wa Mulungu” Uchinjirize Mtima Wanu
    Nsanja ya Olonda—1991
  • Mtendere wa Umulungu Kaamba ka Awo Ophunzitsidwa ndi Yehova
    Nsanja ya Olonda—1987
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2013
w13 6/1 tsamba 16

KUYANKHA MAFUNSO A M’BAIBULO

N’chifukwa chiyani padzikoli palibe mtendere weniweni?

Kuti padzikoli pakhale mtendere weniweni m’pofunika boma limene lingaphunzitse anthu kukhala mwamtendere

Baibulo limapereka zifukwa ziwiri. Chifukwa choyamba n’chakuti anthu sanalengedwe kuti azitha kudzilamulira okha. Chachiwiri n’chakuti “dziko lonse lili m’manja mwa woipayo,” yemwe ndi Satana Mdyerekezi. N’chifukwa chake zimene anthu akhala akuchita kuti abweretse mtendere padziko lonse zalephereka.—Werengani Yeremiya 10:23; 1 Yohane 5:19.

Chinthu chinanso chimene chikuchititsa kuti padzikoli pasakhale mtendere weniweni n’chakuti anthu ndi odzikonda komanso adyera. Kuti padzikoli pakhale mtendere m’pofunika boma limodzi lolamulira dziko lonse, lomwe lingaphunzitse anthu kuti azikonda kuchita zinthu zabwino komanso kuti azikonda anthu anzawo.—Werengani Yesaya 32:17; 48:18, 22.

Ndani adzabweretsa mtendere padzikoli?

Mulungu yemwe ndi Wamphamvuyonse walonjeza kuti adzakhazikitsa boma limene lidzalamulire dziko lonse lapansi. Bomalo lidzathetsa maboma onse a anthu. (Danieli 2:44) Yesu, yemwe ndi Mwana wa Mulungu, adzalamulira monga Kalonga Wamtendere. Iye adzachotsa anthu onse ochita zoipa ndipo adzaphunzitsa anthu kukhala mwamtendere.—Werengani Yesaya 9:6, 7; 11:4, 9.

Panopa, Yesu wayamba kale kuphunzitsa anthu kukhala mwamtendere. Iye akuchita zimenezi potsogolera ntchito yophunzitsa anthu Baibulo imene otsatira ake akuchita padziko lonse lapansi. Posachedwapa, padzikoli padzakhala mtendere weniweni.—Werengani Yesaya 2:3, 4; 54:13.

Kuti mudziwe zambiri, werengani mutu 3 m’buku ili, Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni? lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena