Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 3/01 tsamba 7
  • Zilengezo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zilengezo
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
km 3/01 tsamba 7

Zilengezo

◼ Mabuku ogaŵira mu March: Chidziŵitso Chotsogolera ku Moyo Wosatha. Tidzayesetsa kuyambitsa maphunziro a Baibulo apanyumba. April ndi May: Magazini a Nsanja ya Olonda ndi Galamukani! Paulendo wobwereza mukapeza achidwi, aikeni pandandanda ya anthu amene mumakawagaŵira magazini. Gaŵirani buku la Chidziŵitso kapena bulosha la Mulungu Amafunanji, n’cholinga choyambitsa maphunziro a Baibulo a panyumba. June: Kodi Mulungu Amafunanji kwa Ife? kapena Chidziŵitso Chotsogolera ku Moyo Wosatha. Khalani ndi cholinga choyambitsa maphunziro a Baibulo apanyumba.

◼ Ofalitsa amene akufuna kuchita upainiya wothandiza mu April ayenera kuyamba kukonzekera pakalipano ndipo apereke mafomu awo mwamsanga. Zimenezi zidzathandiza akulu kupanga makonzedwe ofunikira a utumiki wakumunda ndi kupeza magazini ndi mabuku ena okwanira. Lengezani kumpingo mayina a anthu onse omwe avomerezedwa kuchita upainiya wothandiza.

◼ Chikumbutso chidzachitika Lamlungu, pa April 8, 2001. Patsikuli sikudzakhala misonkhano koma kukumana kokonzekera utumiki wakumunda. Akulu angakonze kudzachita phunziro la Nsanja ya Olonda tsiku lina.

◼ Omwe akusonkhana ndi mpingo ayenera kulembetsa magazini a Nsanja ya Olonda ndi Galamukani!, kuphatikizapo makope awoawo, kudzera kumpingo, kaya kulembetsako n’koyamba kapena n’kulembetsanso.

◼ Sosaite siikonzera wofalitsa aliyense payekha oda ya mabuku. Woyang’anira wotsogolera ayenera kukonza chilengezo chimene chiyenera kuperekedwa mwezi uliwonse asanatumize ku Sosaite oda ya mabuku a mpingo ya mwezi ndi mwezi kuti onse ofuna mabuku adziŵitse mbale wosamalira mabuku. Chonde kumbukirani mabuku amene ali paoda yapadera.

◼ Zofalitsa Zatsopano Zimene Zilipo:

Mboni za Yehova—Kodi Iwo Ndani? Kodi Amakhulupirira Chiyani?—Chicheŵa, Chitumbuka

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena