Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb19 April tsamba 2
  • April 1-7

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • April 1-7
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2019
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2019
mwb19 April tsamba 2

April 1-7

1 AKORINTO 7-9

  • Nyimbo Na. 136 ndi Pemphero

  • Mawu Oyamba (Osapitirira 3 min.)

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

  • “Kusakhala Pabanja ndi Mphatso”: (10 min.)

    • 1 Akor. 7:32​—Akhristu omwe sali pabanja amatumikira Yehova popanda kuda nkhawa ndi mavuto amene anthu apabanja amakumana nawo (w11 1/15 18 ¶3)

    • 1 Akor. 7:33, 34​—Akhristu omwe ali pabanja “amadera nkhawa zinthu za dziko” (w08 7/15 27 ¶1)

    • 1 Akor. 7:37, 38​—Akhristu omwe asankha kusakhala pabanja n’cholinga choti achite zambiri potumikira Yehova ‘amachita bwino koposa’ amene ali pabanja (w96 10/15 12-13 ¶14)

  • Kufufuza Mfundo Zothandiza: (8 min.)

    • 1 Akor. 7:11​—Kodi n’chiyani chingachititse Mkhristu kusankha kuti apatukane ndi mwamuna kapena mkazi wake? (lvs 251)

    • 1 Akor. 7:36​—N’chifukwa chiyani Akhristu ayenera kulowa m’banja ‘akapitirira pachimake pa unyamata’? (w00 7/15 31 ¶2)

    • Kodi mwaphunzira zotani zokhudza Yehova pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?

    • Kodi ndi mfundo zina ziti zothandiza zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?

  • Kuwerenga Baibulo: (Osapitirira 4 min.) 1 Akor. 8:1-13 (th phunziro 5)

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI

  • Kuwerenga Komanso Kuphunzitsa Mwaluso: (10 min.) Nkhani yokambirana. Onerani vidiyo yakuti Kunena Mawu Oyenera Musanayambe Kuwerenga Lemba, kenako kambiranani phunziro 4 m’kabuku ka Kuphunzitsa.

  • Nkhani: (Osapitirira 5 min.) w12 11/15 20​—Mutu: Kodi Anthu Amene Amasankha Kusakhala Pabanja Amalandira Mphatsoyi M’njira Yapadera? (th phunziro 12)

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

  • Nyimbo Na. 37

  • Muzigwiritsa Ntchito Bwino Nthawi Yomwe Simuli Pabanja: (15 min.) Onerani vidiyoyi. Kenako kambiranani mafunso otsatirawa: Kodi Akhristu amene sali pabanja amakumana ndi mavuto otani? (1 Akor. 7:39) N’chifukwa chiyani tinganene kuti mwana wa Yefita ndi chitsanzo chabwino? Kodi Yehova amadalitsa bwanji anthu amene amakhalabe okhulupirika? (Sal. 84:11) Kodi abale ndi alongo mumpingo angalimbikitse bwanji Akhristu omwe sali pabanja? Kodi Akhristu omwe sali pabanja ali ndi mwayi wochita mautumiki ati?

  • Phunziro la Baibulo la Mpingo: (30 min.) jy mutu 32

  • Mfundo Zimene Taphunzira Komanso za Mlungu Wamawa (3 min.)

  • Nyimbo Na. 117 ndi Pemphero

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena