Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb20 February tsamba 8
  • February 24–March 1

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • February 24–March 1
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2020
Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2020
mwb20 February tsamba 8

February 24–March 1

GENESIS 20-21

  • Nyimbo Na. 108 ndi Pemphero

  • Mawu Oyamba (Osapitirira 1 min.)

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

  • “Yehova Amakwaniritsa Zomwe Walonjeza”: (10 min.)

    • Gen. 21:1-3​—Sara anatenga pakati ndipo anabereka mwana wamwamuna (wp17.5 14-15)

    • Gen. 21:5-7​—Yehova anapangitsa zinthu zomwe zinkaoneka ngati zosatheka kukhala zotheka

    • Gen. 21:10-12, 14​—Abulahamu ndi Sara ankakhulupirira kwambiri malonjezo a Yehova okhudza Isaki

  • Kufufuza Mfundo Zothandiza: (10 min.)

    • Gen. 20:12​—Kodi Sara anali mlongo wake wa Abulahamu m’njira yotani? (wp17.3 12, mawu a m’munsi.)

    • Gen. 21:33​—Kodi Abulahamu anaitanira bwanji pa “dzina la Yehova”? (w89 7/1 20 ¶9)

    • Kodi mwapeza mfundo ziti zokhudza Yehova, utumiki kapena zinthu zina pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?

  • Kuwerenga Baibulo: (Osapitirira 4 min.) Gen. 20:1-18 (th phunziro 5)

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI

  • Vidiyo ya Ulendo Wobwereza Wachiwiri: (5 min.) Nkhani yokambirana. Onerani vidiyo ndipo kenako funsani omvera mafunso otsatirawa: Kodi wofalitsayu wathandiza bwanji munthuyo kuona mmene angagwiritsire ntchito mfundo ya palemba lomwe awerenga? N’chifukwa chiyani tinganene kuti imeneyi ndi njira yabwino yothandizira munthu amene wasonyeza chidwi?

  • Ulendo Wobwereza Wachiwiri: (Osapitirira 3 min.) Gwiritsani ntchito chitsanzo cha ulendo wobwereza wachiwiri. (th phunziro 4)

  • Phunziro la Baibulo: (Osapitirira 5 min.) bhs 35 ¶19-20 (th phunziro 3)

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

  • Nyimbo Na. 111

  • Lipoti la Chaka Chautumiki: (15 min.) Nkhani yokambidwa ndi mkulu. Pambuyo powerenga chilengezo chochokera ku ofesi ya nthambi chokhudza lipoti la chaka chautumiki, funsani ofalitsa omwe munawasankhiratu kuti afotokoze zinthu zolimbikitsa zimene anakumana nazo mu utumiki chaka chathachi.

  • Phunziro la Baibulo la Mpingo: (30 min.) jy mutu 74

  • Mfundo Zimene Taphunzira Komanso za Mlungu Wamawa (3 min.)

  • Nyimbo Na. 100 ndi Pemphero

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena