Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb20 June tsamba 8
  • Mungathe Kulalikira Komanso Kuphunzitsa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mungathe Kulalikira Komanso Kuphunzitsa
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2020
  • Nkhani Yofanana
  • Zimene Tingachite Kuti Tizisangalalabe Utumiki Wathu Ukasintha
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2019
  • Yehova Akutiphunzitsa Kuti Tigwire Ntchitoyi
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
  • ‘Limba Mtima Ndipo Ugwire Ntchitoyi’
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2017
  • Musalephere Kulalikira
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2020
mwb20 June tsamba 8

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Mungathe Kulalikira Komanso Kuphunzitsa

Mose atangopatsidwa kumene utumiki ndi Yehova, ankadziona kuti sangakwanitse. (Eks. 4:10, 13) Kodi inunso munayamba mwamvapo choncho? Kodi mukuphunzira Baibulo ndi a Mboni za Yehova? Kodi mumadzifunsa ngati mungakwanitse kulalikira kunyumba ndi nyumba? Kapena ndinu wachinyamata ndipo mumachita mantha kulalikira kusukulu. Kapenanso mwina mumachita mantha kulalikira m’malo opezeka anthu ambiri kapena kuchita ulaliki wa patelefoni. Pemphani Yehova kuti akupatseni mzimu wake woyera. (1 Pet. 4:11) Muzikhulupirira kuti angakuthandizeni kukwaniritsa utumiki uliwonse umene wakupatsani.​—Eks. 4:11, 12.

ONERANI VIDIYO YAKUTI MUZICHITA ZINTHU MOLIMBA MTIMA​—OFALITSA, NDIPO KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • Kodi Mlongo Aoyama anakumana ndi vuto lotani?

  • N’chiyani chinamuthandiza kupeza mphamvu komanso kukhala olimba mtima?​—Yer. 20:7-9

  • Kodi kuchita zambiri potumikira Yehova kunamuthandiza bwanji?

  • Kodi Yehova angakuthandizeni kuthana ndi mavuto ati mukamalalikira?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena