Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g90 5/8 tsamba 3
  • Dziko Laudongo Tikulifunadi

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Dziko Laudongo Tikulifunadi
  • Galamukani!—1990
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Ngozi—Kuipitsa
  • Mulungu Amakonda Anthu Oyera
    Kodi Mungatani Kuti ‘Mulungu Apitirize Kukukondani’?
  • Kodi Ukhondo Ndi Wofunika Motani?
    Nsanja ya Olonda—2002
  • Yehova Amakonda Anthu Aukhondo
    Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2019
  • Yehova Amafuna Kuti Anthu Ake Akhale Oyera
    Kodi Mungatani Kuti Mulungu Azikukondani?
Onani Zambiri
Galamukani!—1990
g90 5/8 tsamba 3

Dziko Laudongo Tikulifunadi

Ndi mlembi wa Galamukani! mu Britain

KODI mudadziŵa kuti oyendetsa matekisi a mu London ali ndi lamulo la kusunga matekisi awo kukhala audongo? Kulephera kutero kungatulukepo kuwaletsa kuyenda m’makwalala a mzindawo kwa nyengo yanthaŵi. Ngakhale pamene mikhalidwe ya msewu iri yoipa ndipo magalimoto ambiri amakhala akuda kwa masiku ambiri, tekisi ya ku London imakhala yaudongo kopambana. Mawonekedwe owala a galimotowo amadzutsa mwa woyendetsayo ndi okweramo ake malingaliro a kunyadira ndi chisangalalo.

Mofananamo, pamene nyumba yathu, zovala zathu, ndi zinthu zathu ziri zaudongo, zimachititsa mwa ife malingaliro a mkhalidwe wabwino. Zimaipira mnyamata wa sukulu amene amayi ake amuwona akuloŵa m’nyumba nasiya nkukuluzi ya matope a ku nsapato zake zakuda pakapeti!

Ndiiko komwe, umoyo wabwino umadalira kwakulukulu pa udongo waumwini. Matupi athu amafuna chisamaliro ndi kusamba kokhazikika kuchotsa litsiro limene lingaloŵerepo matenda. Makampani amalonda amapeza mapindu aakulu mwakugulitsa zoyeretsera, zochapira, polishi, sopo, shampuu, ndi zophera tizirombo zimene timagwiritsira ntchito kudzisunga ife eni ndi malo otizinga kukhala audongo. Ndithudi, anthu ambiri ali ozindikira za kufunika kwa udongo. Koma ngati mukukhala mumzinda, mukudziŵa kuti sizokhazi.

Ngozi—Kuipitsa

Okhala mumzinda amadziŵa bwino lomwe za kuipitsa ndi malo owazinga odetsedwa. Iwo amakuwona m’zinyatsi zosatoledwa, m’zinyalala zosiidwa mosasamala pamakwalala, ndi m’zolembalemba zodetsa pa nyumba zapoyera. Iwo amakununkhiza mu utsi wotsamwitsa wochokera ku magalimoto ochuluka ndi mpweya wautsi wonunkha umene umakuta mizinda ina.

Mwinamwake ndicho chifukwa chake ambiri okhala m’mizinda amayesa nthaŵi zina kukathera nthaŵi ku malo akumidzi. Iwo amasangalala kupumira m’mapapo awo mpweya waudongo, mwinamwake ngakhale kumwa madzi oyera mbee a mu mfuleni wochokera m’phiri. Ena amakonda kupita kugombe ndi kumapuma pa mchenga kapena kuziziritsa thupi mwakusamba kosangalatsa pa nyanja.

Ngakhale nditero, taimani pang’ono! Litsiro ndi kuipitsa zikubisala kumenekonso. Inu mungafunse kuti ‘zingatero motani?’ ‘Akuwoneka awudongo.’ Chabwino, tiyeni tiyang’anitsitse pang’ono pa mpweya “waudongowo” ndi madzi “oyerawo.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena