Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g95 8/8 tsamba 3
  • Pamene Kwagwa Tsoka

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Pamene Kwagwa Tsoka
  • Galamukani!—1995
  • Nkhani Yofanana
  • Masoka Achilengedwe—Kodi Mulungu Ndiye Amawachititsa?
    Nsanja ya Olonda—1993
  • Kodi Baibulo Limanena Zotani pa Nkhani ya Ngozi Zadzidzidzi?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Kodi Baibulo Linaneneratu Zotani pa Nkhani ya Zivomerezi Zamphamvu?
    Nkhani Zina
  • Masoka Achilengedwe—Kodi Ali Chizindikiro cha Nthaŵi?
    Nsanja ya Olonda—1993
Onani Zambiri
Galamukani!—1995
g95 8/8 tsamba 3

Pamene Kwagwa Tsoka

M’ZAKA za zana la 20 mwachitika masoka aakulu, ndipo munthu ndiye amene wachititsa ambiri a iwo. Komabe, ena sindiye wawachititsa. Polosera za masiku athu, Yesu Kristu anati: “Mtundu umodzi wa anthu udzaukirana ndi mtundu wina, ndi ufumu ndi ufumu wina; ndipo kudzakhala njala ndi zivomezi m’malo akutiakuti.” (Mateyu 24:7) Zoona, munthu ali ndi mlandu wochititsa nkhondo ndi njala, koma sindiye amachititsa zivomezi. Mofanana ndi zimenezo, pamene kuli kwakuti zochita za munthu zachititsa kusefukira kwa madzi kowononga m’malo ena, iye sangaimbidwe mlandu wochititsa zivomezi. Ngakhale mikuntho ndi kuphulika kwa mavolokano si mlandu wa munthu.

Kaya akhale otani, masoka achilengedwe amasonyeza kuchepa kwa munthu, kupanda kwake mphamvu pamene akumana ndi mphamvu zazikulu zowopsa zachilengedwe. Nthaŵi zambiri, dzikoli, mudzi wathuwu, limamveka kukhala losungika ndi lolimba kwambiri. Koma pamene ligwedezeka ndi chivomezi, kukokololedwa ndi madzi osefukira, kapena kuwombedwa ndi mphepo zolimba zimene zimalikantha kosaleka ngati kuti pali kuphulika kwamphamvu, mkhalidwewo wa chisungiko umazimirira.

Masoka achilengedwe awononga zinthu kwambiri ndi kutayitsa miyoyo yochuluka m’zaka za zana la 20. Kodi zimenezi zikanapeŵeka? Kodi pali zilizonse zimene zingachitidwe kuchepetsa zotulukapo zake zosakazazo? Kodi ife patokha tingachitenji kuti tidzitetezere? Kodi timasoŵeratu chochita kutagwa tsoka? Kodi anthu adzavutikabe chonchi? Nkhani zotsatira zidzayankha mafunso ameneŵa.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena