Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g96 4/8 tsamba 22
  • Kupita Patsogolo ndi Manja Amene Amapereka Zizindikiro

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kupita Patsogolo ndi Manja Amene Amapereka Zizindikiro
  • Galamukani!—1996
  • Nkhani Yofanana
  • ‘Yehova Wawalitsa Nkhope Yake pa Iwo’
    Nsanja ya Olonda—2009
  • Muziona Kuti Abale ndi Alongo Anu Osamva Ndi Ofunika Kwambiri
    Nsanja ya Olonda—2009
  • “Kuphunzira Baibulo Kukuthandiza Anthu Osamva”
    Galamukani!—2010
  • Munthu Woyamba wa Chinenero Chamanja Kuphunzira Baibulo
    Buku Lapachaka la Mboni za Yehova la 2015
Onani Zambiri
Galamukani!—1996
g96 4/8 tsamba 22

Kupita Patsogolo ndi Manja Amene Amapereka Zizindikiro

KUYAMBIRA mu June 1995 ndi kupitiriza m’chilimwe chonse, Mboni za Yehova m’gawo la nthambi ya United States, zinakhala ndi misonkhano yachigawo 181 yokhala ndi mutu wakuti “Atamandi Achimwemwe.” Pa iŵiri ya imeneyi—umodzi kummaŵa ndipo wina kummadzulo—programu yonse inachitidwa mwachindunji mu American Sign Language (Chinenero Cholankhula ndi Manja cha ku America.) Motero programuyo inamveketsedwa bwino kwambiri—nkhani yokambidwa mwachindunji kwa agonthi m’chinenero cholankhula ndi manja imamveka bwino kwambiri kuposa kumasulira mawu onenedwa.

Nthumwi zinalipo zochokera ku mipingo 11 yachinenero cholankhula ndi manja ndi magulu ena pafupifupi 30 achinenero cholankhula ndi manja ochokera mu United States yense. Koma enanso amene analipo anali nthumwi zochokera ku Britain, Canada, Denmark, Dominican Republic, Ecuador, Germany, Japan, Mexico, Norway, Puerto Rico, ndi Russia. Motero, panali mkhalidwe wa kumaiko osiyanasiyana.

Mawailesi a kanema analinganizidwa kotero kuti programuyo ionekere pamawailesi akanema olunzanitsidwa ndi waya. Komabe, nthumwi zingapo zinali ponse paŵiri agonthi ndi akhungu. Kodi anthuŵa anapindula motani ndi programuyo? Kunali kogwiradi mtima kuona antchito odzifunira oposa zana limodzi akumasinthana kuwauza iwo programu ya tsiku lililonse mwa kumasulira kwa tactile (kukhudza).

Pamisonkhano iŵiri imeneyi, 36 anasonyeza kudzipatulira kwawo kwa Yehova Mulungu mwa ubatizo. Chochitika china chapadera chinali drama yakuti, Kuchitira Ulemu Owuyenerera m’Zaka Zawo Zaukalamba. Mmene kunalili kosangalatsa kuchita drama yonseyi m’chinenero cholankhula ndi manja, ikumalola agonthi kukhalamo ndi mbali yaikulu m’chochitikacho!

Ndiyeno panatulutsidwa buku latsopano lothandizira kuphunzira Baibulo, Knowledge That Leads to Everlasting Life. Osonkhanawo anasangalala makamaka kudziŵa kuti buku limenelo linali kupangidwa m’chinenero cholankhula ndi manja pa matepu a vidiyo! Voliyumu 1, imene inatulutsidwa pamsonkhanopo, ili ndi machaputala atatu oyambirira. Mavoliyumu ena asanu adzatsatira. “Tiyamikira kwambiri kaamba ka vidiyo yatsopanoyi,” inatero nthumwi yochokera ku Ohio. “Idzatithandizira kufulumiza ntchito polalikira kwa agonthi.”

Amene analipo 2,621 pamisonkhano iŵiriyi anapita kwawo atatsitsimulidwa mwauzimu. Kuposa ndi kale lonse, anali otsimikiza kunenanso mawu a wamasalmo akuti: “Zonse zakupuma zilemekeze Yehova. Haleluya.”—Salmo 150:6, NW.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena