Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g01 3/8 tsamba 11
  • Kuona Mbalame N’kosangalatsa Kwambiri

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kuona Mbalame N’kosangalatsa Kwambiri
  • Galamukani!—2001
  • Nkhani Yofanana
  • Mbalame Zimawomba Nyumba Mwangozi
    Galamukani!—2009
  • “Onetsetsani Mbalame”
    Galamukani!—2014
  • Kodi Mbalame Ingam’phunzitsenji Mkaidi?
    Galamukani!—2000
Galamukani!—2001
g01 3/8 tsamba 11

Kuona Mbalame N’kosangalatsa Kwambiri

DZIKO lopanda mbalame silingasangalatse! Kulira kwake, nyimbo zake, mitundu yake yosiyanasiyana ndiponso kuuluka kwake—zonsezi n’zosangalatsadi. Koma kodi n’kangati pamene timamvetsera kapena kuyang’ana mbalame? Ngati m’makhala mumzinda umene anthu amakhala piringupiringu tsiku n’tsiku komanso waphokoso la magalimoto, ndiye kuti simungadziŵe n’komwe mbalame zomwe m’makhala nazo pafupi. Ngakhale ngati m’makhala kumidzi, n’kwapafupi kusachita nazo chidwi. Koma kodi mungakonde kuzionera pafupi mbalame za m’dera lanu?

Mungachite zimenezi mwa kuziwazira chakudya kuseri kwa nyumba yanu pafupi ndi zenera. Kenako, tengani chipangizo choonera zinthu patali kapena imani pazeneralo—ndipo khalani phee! Tengani kamera yamphamvu ndiponso filimu yokwanira yonjambulika mofulumira. Tenganinso buku lofotokoza mbalame ngati muli nalo kuti muthe kuzidziŵa bwinobwino. Kenako, yang’anitsitsani, mvetserani, ndipo sangalalani!

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena