Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 6/10 tsamba 11-31
  • Zoti Banja Likambirane

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zoti Banja Likambirane
  • Galamukani!—2010
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Zinachitikira Kuti?
  • KODI MUKUDZIWA CHIYANI ZOKHUDZA MFUMU HEZEKIYA?
  • ZITHUNZI ZOTI ANA APEZE
  • KUCHOKERA M’MAGAZINI INO
  • MAYANKHO A MAFUNSO A PATSAMBA 31
  • Kodi Mungayankhe Bwanji?
    Galamukani!—2008
  • Zoti Banja Likambirane
    Galamukani!—2010
  • Zoti Banja Likambirane
    Galamukani!—2010
  • Kodi Mungayankhe Bwanji?
    Galamukani!—2009
Onani Zambiri
Galamukani!—2010
g 6/10 tsamba 11-31

Zoti Banja Likambirane

Zinachitikira Kuti?

1. Kodi izi zinachitikira pafupi ndi mzinda uti?

ZOKUTHANDIZANI: Werengani Machitidwe 6:7-9; 7:54-60.

Lembani mzere wozungulira yankho lanu pamapu awa.

Damasiko

Yerusalemu

Betelehemu

2. Kodi Sitefano akugendedwa chifukwa chiyani?

․․․․․

3. Kodi Sitefano anapempha kuti Mulungu awachitire chiyani anthu amene amamugendawo?

․․․․․

KAMBIRANANI:

Kodi zimene Sitefano anachitira anthuwo mukuziona bwanji? Mukanakhala inuyo kodi mukanatani, ndipo n’chifukwa chiyani mukanachita zimenezo?

KODI MUKUDZIWA CHIYANI ZOKHUDZA MFUMU HEZEKIYA?

4. Kodi bambo ake a Hezekiya anali ndani?

ZOKUTHANDIZANI: Werengani 2 Mafumu 18:1.

․․․․․

5. Ngakhale kuti bambo a Hezekiya anali oipa kwambiri, kodi Hezekiya anali ndi mbiri yotani?

ZOKUTHANDIZANI: Werengani 2 Mafumu 18:5.

․․․․․

KAMBIRANANI:

Kodi n’chiyani chinathandiza Hezekiya kukhalabe ndi chikhulupiriro cholimba?

ZOKUTHANDIZANI: Werengani 2 Mafumu 18:6.

Ngati m’bale wanu atasiya kutumikira Mulungu, kodi mungatsanzire bwanji Hezekiya?

ZITHUNZI ZOTI ANA APEZE

Pezani zithunzi izi m’magazini ino. Fotokozani zimene zikuchitika pa chithunzi chilichonse.

KUCHOKERA M’MAGAZINI INO

Yankhani mafunsowa, ndipo lembani vesi kapena mavesi a m’Baibulo omwe akusowapo.

TSAMBA 5 Kodi mmene thupi lathu limagwirira ntchito zimatsimikizira chiyani? Salmo 139:․․․

TSAMBA 8 Kodi mtendere wa Mulungu ungatichitire chiyani? Afilipi 4:․․․

TSAMBA 13 Kodi kupuma pang’ono kuli bwino kuposa chiyani? Mlaliki 4:․․․

TSAMBA 23 Kodi Mulungu amakonda munthu wotani? 2 Akorinto 9:․․․

● Mayankho ali patsamba 11

MAYANKHO A MAFUNSO A PATSAMBA 31

1. Yerusalemu.

2. Sitefano akuimbidwa mlandu wochitira mwano Mulungu.

3. Mulungu awakhululukire.

4. Mfumu Ahazi.

5. Panalibenso mfumu ina kupatula iyeyu imene inali yodzipereka kwambiri pa kulambira koona.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena