Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g20 No. 2 tsamba 8-9
  • Kodi Mavuto Athu Timawachititsa Tokha?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Mavuto Athu Timawachititsa Tokha?
  • Galamukani!—2020
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Chifukwa Chake Kudziwa Yankho la Funsoli Kuli Kofunika
  • Taganizirani Izi
  • Zimene Baibulo Limanena
  • Kodi Baibulo Limanena Zotani?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2017
  • Nkhani Zimene Zili M’magaziniyi
    Galamukani!—2020
  • Funso Lachitatu: N’chifukwa Chiyani Mulungu Amalola Kuti Ndizivutika?
    Nsanja ya Olonda—2012
  • N’chifukwa Chiyani Anthu Akuvutika Chonchi?
    Galamukani!—2011
Onani Zambiri
Galamukani!—2020
g20 No. 2 tsamba 8-9
Bambo wakhala pampando m’nyumba mwake ndipo wanyamula ndudu ya fodya komanso botolo la mowa.

2. Kodi Mavuto Athu Timawachititsa Tokha?

Chifukwa Chake Kudziwa Yankho la Funsoli Kuli Kofunika

Ngati yankho ndi lakuti inde, ndiye kuti tikhoza kukwanitsa kuchepetsako mavuto athu.

Taganizirani Izi

Kodi anthu achititsa mavuto otsatirawa kufika pati?

  • Kachithunzi ka chibakera, komwe kakuimira nkhanza.

    Nkhanza.

    Bungwe Loona za Umoyo pa Dziko Lonse linanena kuti munthu mmodzi pa anthu 4 alionse, anachitiridwapo zinthu zankhanza ali wamng’ono, ndipo mzimayi mmodzi pa azimayi atatu alionse anachitiridwapo zankhanza kapena kugwiriridwa pa nthawi inayake.

  • Kachithunzi ka ziliza, zomwe zikuimira manda.

    Kuferedwa.

    Lipoti la Bungwe Loona za Umoyo pa Dziko Lonse la mu 2018, linanena kuti “anthu pafupifupi 477,000 anaphedwa padziko lonse mu 2016.” Zimenezi zikuwonjezera pa anthu pafupifupi 180,000 omwe akuganiziridwa kuti anaphedwa pa nkhondo ndi zipolowe m’chaka chomwecho.

  • Kachithunzi ka mtima, komwe kakuimira matenda.

    Matenda.

    Fran Smith, yemwe analemba nkhani ina mu magazini ya National Geographic ananena kuti: “Anthu oposa 1 biliyoni amasuta, ndipo fodya ali m’gulu la zinthu zomwe zikuyambitsa matenda 5 akuluakulu amene akupha anthu. Matendawa ndi sitiroko, matenda a mtima, chifuwa, matenda a m’mapapo ndi khansa ya m’mapapo.”

  • Kachithunzi ka sikelo yomwe ikulemera mbali imodzi, zomwe zikuimira tsankho.

    Tsankho.

    Katswiri wina wa zamaganizo dzina lake Jay Watts ananena kuti: “Umphawi, kusalana, kusankhana mitundu, kuona kuti akazi ndi osafunika, kuthawa m’dera lomwe ukukhala komanso mtima wampikisano, zikuchititsa anthu kudwala matenda ovutika maganizo.”

    KUTI MUDZIWE ZAMBIRI

    Onerani vidiyo yakuti N’chifukwa Chiyani Mulungu Analenga Dziko Lapansi? pa jw.org

Zimene Baibulo Limanena

Bambo yemwe amasuta fodya komanso kumwa mowa uja wagona pabedi kuchipatala. Mkazi wake wayang’ana kumbali pamene dokotala akufotokoza kuti thanzi la mwamuna wake silili bwino.

Anthu ndi amene amayambitsa mavuto ambiri omwe timakumana nawo.

Ena mwa mavutowa amayamba ndi maboma ankhanza, zomwe zimachititsa kuti anthu amene amawalamulira azivutika kwambiri.

“Munthu wapweteka munthu mnzake pomulamulira.”​—MLALIKI 8:9.

Kuvutika kukhoza kuchepetsedwa.

Mfundo za m’Baibulo zimalimbikitsa anthu kukhala ndi moyo wathanzi komanso kukhala mwamtendere ndi anthu ena.

“Mtima wodekha ndiwo moyo wa munthu, koma nsanje imawoletsa mafupa.”—MIYAMBO 14:30.

“Kuwawidwa mtima konse kwa njiru, kupsa mtima, mkwiyo, kulalata ndiponso mawu achipongwe zichotsedwe mwa inu limodzi ndi zoipa zonse.”​—AEFESO 4:31.

Kodi mavuto athu timawachititsa tokha?

Baibulo limanena kuti: “Chilichonse chimene munthu wafesa, adzakololanso chomwecho.” (Agalatiya 6:7) Mavuto ena amayamba chifukwa cha zosankha zathu. N’chifukwa chake madokotala amalimbikitsa anthu kuti azidya zakudya zopatsa thanzi, azichita masewera olimbitsa thupi komanso azipewa zinthu zimene zingaike moyo wawo pangozi, ngati kusuta. Komabe, sizingakhale zoona kunena kuti mavuto onse amayambitsidwa ndi anthu. Anthu ambiri osalakwa akuvutika ndi ngozi komanso mavuto ena.

N’chifukwa chiyani anthu abwino amavutika?

Onani funso 3.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena