Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 47
  • Mbala mu Israyeli

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mbala mu Israyeli
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Mfundo Zazikulu za M’buku la Yoswa
    Nsanja ya Olonda—2004
  • Zimene Yoswa Anakumbukira
    Nsanja ya Olonda—2002
  • Usakhale Wakuba!
    Phunzirani kwa Mphunzitsi Waluso
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 47

NKHANI 47

Mbala mu Israyeli

ONANI chimene chikukwiriridwa ndi mwamuna’yu m’hema mwake! Mwainjiro wokongola, mkute wa golidi ndi timiyala ta siliva. Iye anazitenga m’Yeriko. Koma kodi paja zinthu za m’Yeriko anati zichitidwenji? Kodi mukukumbukira?

Izo zinayenera kuonongedwa, golidi ndi siliva n’kukasungidwa mosungira chuma m’chihema cha Yehova. Anthu’wa anyozatu Mulungu. Aba za Mulungu. Dzina la munthu’yu ndiro Akani, ndipo ali nayewo ndiwo ena a m’banja lake. Tiyeni tione zimene zikuchitika.

Akani ataba zinthu’zi, Yoswa akutumiza amuna ena kukamenyana ndi mzinda wa Ai. Koma akugonjetsedwa m’nkondo. Ena akuphedwa, otsala’wo nathawa. Yoswa ali n’chisoni kwambiri. Akugona chafufumimba napemphera kwa Yehova: ‘Mwaloleranji izi kutichitikira?’

Yehova akuyankha kuti: ‘Nyamuka! Israyeli wachimwa. Iwo atenga zinthu zoyenera kuonongedwa kapena kuperekedwa ku chihema cha Yehova. Aba mwiinjiro wokongola naubisa. Sindidzakudalitsani kufikira mutauononga, ndi wotenga zinthu’zi.’ Yehova akuti adzasonyeza Yoswa munthu woipa’yu.

Chotero Yoswa akusonkhanitsa anthu onse, Yehova nasonyeza Akani woipa’yo. Akani akuti: ‘Ndachimwa. Ndinaona mwiinjiro wokongola, ndi mkute wa golidi ndi timiyala ta siliva. Ndinazifuna kwambiri kwakuti ndinazitenga. Mudzazipeza zitakwiriridwa m’hema wanga.’

Zitapezeka zinthu’zi ndi kuperekedwa kwa Yoswa, akuti kwa Akani: ‘Watibvutitsiranji? Tsopano Yehova adzabvutitsa iwe!’ Pompo anthu onse anapha Akani ndi banja lake mwa kuwaponya miyala. Kodi izi sizikusonyeza kuti tisamatenga zinthu zosakhala zathu?

Pambuyo pake Israyeli akupita ku nkhondo kukamenyana’nso ndi Ai. Pa nthawi ino Yehova akuthandiza anthu ake napambana.

Yoswa 7:1-26; 8:1-29.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena