Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 59
  • Chifukwa chake Davide Akuthawa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Chifukwa chake Davide Akuthawa
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Davide ndi Sauli
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Davide Akulongedwa Ufumu
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Zimene Zili Mʼbuku la 1 Samueli
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Mafunso Ochokera kwa Owerenga
    Nsanja ya Olonda—2007
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 59

NKHANI 59

Chifukwa chake Davide Akuthawa

DAVIDE atapha Goliati, mkulu wankhondo wa Israyeli Abineri akumka naye kwa Sauli. Sauli ali wokondwera kwambiri ndi Davide. Akum’panga kukhala mkulu m’gulu lake la nkhondo nam’tengera ku nyumba ya mfumu.

Kenako, pobwera ku nkhondo komenyana ndi Afilisti, akazi akuyimba kuti: ‘Sauli anapha zikwi zochuluka, koma Davide zikwi makumi ambiri.’ Izi zikuchititsa nsanje Sauli, chifukwa Davide akupatsidwa ulemu waukulu koposa iye. Mwana wake Jonatani sali ndi nsanje. Akukonda kwambiri Davide, naye’nso Davide akum’konda. Chotero awiri’wa akupangana pangano la kukhala mabwenzi nthawi zonse.

Davide ngwoimba bwino kwambiri zeze, ndipo Sauli amakonda nyimbo zake. Koma tsiku lina nsanje ya Sauli ikum’chititsa kuchita chinthu choopsya. Davide akuyimba zeze, Sauli akutenga mkondo wake nauponya, nati: ‘Ndidzam’pyoza kum’phatikiza ndi khoma!’ Koma iye akulewa, ndipo mkondo’wo ukulasa padera. Kenako Sauli akuphonya Davide ndi mkondo wake kachiwiri. Tsono Davide akudziwa kuti ayenera kukhala wosamala.

Kodi mukukumbukira lonjezo limene Sauli anapanga? Iye anati akapatsa mwana wake wamkazi kwa munthu amene akapha Goliati. Sauli potsiriza akuuza Davide kuti angatenge mwana wake Mikala, koma choyamba akaphe adani Achifilisti 100. Tazilingalirani! Sauli akulingalira kweni-kweni kuti iwo adzapha Davide. Koma sakutero, chotero akupereka mwana wake wamkazi kukhala mkazi wa Davide.

Tsiku lina Sauli akuuza Jonatani ndi atumiki ake onse kuti akufuna kupha Davide. Koma Jonatani akuti: ‘Musabvulaze Davide. Sanachite choipa chiri chonse kwa inu. M’malo mwake, chiri chonse chimene wachita chakhala chothandiza kwa inu. Iye anaika moyo wake pangozi pamene anapha Goliati, ndipo pochiona, munakondwera.’

Sauli akumvera mwana wake, nalonjeza kusam’bvulaza. Davide akubwezeredwamo, natumikira Sauli m’nyumba mwake monga kale. Komabe, tsiku lina, Davide akuyimba nyimbo, Sauli akuponya’nso mkondo wake kwa Davide. Iye akuulewa, mkondo’wo nulasa khoma. N’kachitatu aka! Davide akudziwa kuti ayenera kuthawa tsopano!

Usiku womwewo akumka ku nyumba yake. Koma Sauli akutuma anthu kukam’pha. Mikala akudziwa zimene atate wake walinganiza kuchita. Chotero akuuza mwamuna wake kuti: ‘Ngati suchoka usiku uno, udzakhala utafa m’mawa.’ Usiku’wo Mikala akuthandiza Davide kutulukira pa zenera. Kwa zaka zisanu ndi ziwiri Davide ayenera kubisala m’malo osiyana-siyana kuti Sauli asam’peze.

1 Samueli 18:1-30; 19:1-18.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena