Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 74
  • Munthu Wosaopa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Munthu Wosaopa
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Yeremiya Sanasiye Kulankhula za Yehova
    Phunzitsani Ana Anu
  • Kutumikira Mulungu “M’masiku Otsiriza”
    Zimene Mulungu Akutiuza Kudzera mwa Yeremiya
  • Yehova Anauza Yeremiya Kuti Azilalikira
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • “Ndaika Mawu Anga M’kamwa Mwako”
    Zimene Mulungu Akutiuza Kudzera mwa Yeremiya
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 74

NKHANI 74

Munthu Wosaopa

ONANI anthu’wo akuseka mnyamata’yu. Kodi mukum’dziwa? Uyu ndi Yeremiya. Iye ndi mneneri wofunika kwambiri wa Mulungu.

Chotero pamene Yosiya wangoyamba kumene kuononga mafano m’dziko’lo, Yehova akuuza Yeremiya kukhala mneneri Wake. Komabe, iye akuganiza kuti akali mwana wosati n’kukhala mneneri. Koma Yehova akuti Iye adzam’thandiza.

Iye akuuza Aisrayeli kuleka kuchita zoipa. ‘Milungu imene anthu a dziko amailambira ndi yonyenga,’ akutero. Koma Aisrayeli ambiri akakonda kulambira mafano koposa kulambira Mulungu woona Yehova. Pamene Yeremiya akuuza anthu’wo kuti Mulungu adzawalanga chifukwa cha kuipa kwao, akungom’seka.

Zaka zambiri zikupitapo. Yosiya akufa, ndipo patapita miyezi itatu mwanake Yehoyakimu akukhala mfumu. Yeremiya akuuzabe anthu kuti: ‘Yerusalemu adzaonongedwa ngati simusintha njira zanu zoipa’zi.’ Ansembe akugwira Yeremiya napfuula kuti: ‘Uyenera kuphedwa chifukwa cha kunena izi.’ Ndiyeno akuuza akalonga a Israyeli kuti: ‘Yeremiya ayenera kuphedwa, chifukwa walankhula motsutsa mzinda wathu.’

Kodi iye adzachitanji tsopano? Sakuopa! Iye akuuza onse’wo kuti: ‘Yehova ananditumiza kudzakuuzani zinthu’zi. Ngati simusintha njira zanu za kakhalidwe, Yehova adzaononga Yerusalemu. Koma dziwani izi: Mukandipha, mudzakhala mukupha munthu wosalakwa.’

Akalonga akulola Yeremiya kukhalabe ndi moyo, koma Aisrayeli sakusintha njira zao zoipa. Kenako Nebukadinezara, mfumu ya Babulo, akudza kudzamenyana ndi Yerusalemu. Potsiriza iye akupanga Aisrayeli kukhala akapolo ake. Iye akutenga zikwi zochuluka kumka nazo ku Babulo. Taganizirani m’mene zikakhalira kutengedwa ndi anthu osawadziwa kumka ku dziko lachilendo!

Yeremiya 1:1-8; 10:1-5; 26:1-16; 2 Mafumu 24:1-17.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena