Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 80
  • Anthu a Mulungu Atuluka m’Babulo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Anthu a Mulungu Atuluka m’Babulo
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Koresi Wamkulu
    Galamukani!—2013
  • Kudalira Thandizo la Mulungu
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Dzanja Linalemba Pakhoma
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Buku Limene Mungathe Kulikhulupirira—Gawo 4
    Galamukani!—2011
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 80

NKHANI 80

Anthu a Mulungu Atuluka m’Babulo

PAFUPI-FUPI zaka ziwiri zapitapo chigonjetsedwere Babulo ndi Amedi ndi Aperisi. Ndipo onani zimene zikuchitika tsopano! Aisrayeli akuchoka ku Babulo. Kodi anamasuka motani? Ndani akuwalola kupita?

Koresi, mfumu ya Perisiya ndiyo. Kale-kale Koresi asanabadwe, Yehova anachititsa mneneri wake Yesaya kulemba za iye kuti: ‘Udzachita zimene ndikufuna kuti uchite. Zipata zidzakhala chitsegukire kuti ulande mzinda’wo.’ Ndipo Koresi anatsogolera m’kulanda Babulo. Amedi ndi Aperisi analowa mu mzinda’wo usiku kulowera pa zipata zimene zinasiyidwa zosatseka.

Koma mneneri wa Yehova Yesaya ananena’nso kuti Koresi adzalamulira kuti Yerusalemu ndi kachisi wake zimangidwe’nso. Kodi Koresi anapereka lamulo limene’li? Inde. Nazi zimene iye akuuza Aisrayeli: ‘Pitani, tsopano, ku Yerusalemu ndi kukamanga kachisi wa Yehova, Mulungu wanu.’ Ndipo ndizo zimene Aisrayeli akumka kukachita.

Koma si Aisrayeli onse m’Babulo akatha kuyenda ulendo wautali wobwerera ku Yerusalemu’wo. Ndi ulendo wautali kwambiri wa mamailo pafupi-fupi 500 (makilomita 800) ndipo ambiri ngokalamba kapena odwala kwambiri kosati n’kuyenda kutali. Ndipo pali zifukwa zina zimene ena sakumkera. Koresi akuuza awo amene sakumka kuti: ‘Patsani siliva ndi golidi ndi mphatso zina awo amene akubwerera kukamanga Yerusalemu ndi kachisi wake.’

Chotero mphatso zambiri zikuperekedwa kwa iwo amene akubwerera ku Yerusalemu. Ndipo’nso, Koresi akuwapatsa mbale ndi zikho zimene Nebukadinezara anazitenga m’kachisi pamene anaononga Yerusalemu. Anthu’wo ali ndi zinthu zonyamula zochuluka pobwerera.

Atayenda kwa pafupi-fupi miyezi inai, iwo akufika ku Yerusalemu pa nthawi yake. Zangokwana zaka 70 chiyambire pamene mzinda’wo unaonongedwa, ndipo dziko’lo linasiyidwa labwinja kotheratu. Koma ngakhale Aisrayeli abwerera ku dziko lakwao adzakhala ndi nthawi zobvuta, monga momwe tidzaonera.

Yesaya 44:28; 45:1-4; Ezara 1:1-11.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena