Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • gf phunziro 3 tsamba 5
  • Muyenera Kuphunzira za Mulungu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Muyenera Kuphunzira za Mulungu
  • Mungathe Kukhala Bwenzi la Mulungu!
  • Nkhani Yofanana
  • Yehova Akhoza Kukhala Mnzanu
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
  • Mulungu Akukuitanani Kuti Mukhale Bwenzi Lake
    Mungathe Kukhala Bwenzi la Mulungu!
  • Mmene Mungapezere Chipembedzo Choona
    Mungathe Kukhala Bwenzi la Mulungu!
  • Mmene Mungapezere Mabwenzi
    Nsanja ya Olonda—2000
Onani Zambiri
Mungathe Kukhala Bwenzi la Mulungu!
gf phunziro 3 tsamba 5

PHUNZIRO 3

Muyenera Kuphunzira za Mulungu

Kuti mukhale bwenzi la Mulungu, muyenera kuphunzira za iye. Kodi mabwenzi anu amalidziŵa dzina lanu ndipo amalitchula? Inde amatero. Mulungunso amafuna kuti dzina lake mulidziŵe ndi kumalitchula. Dzina la Mulungu ndi Yehova. (Salmo 83:18; Mateyu 6:9) Muyenera kudziŵanso zimene amafuna ndi zimene safuna. Mufunikiranso kudziŵa mabwenzi ake ndi adani ake. Komatu kudziŵa munthu kumatenga nthaŵi. Baibulo limanena kuti n’kwanzeru kupatula nthaŵi yophunzira za Yehova.—Aefeso 5:15, 16.

Mabwenzi a Mulungu amachita zimene zimam’kondweretsa. Taganizirani za mabwenzi anu. Ngati inuyo muwachitira zoipa ndiponso kuchita zinthu zimene iwo amadana nazo, kodi adzapitiriza kukhala mabwenzi anu? Ndithudi ayi! Mofananamo, ngati mukufuna kukhala bwenzi la Mulungu, muyenera kuchita zimene zimam’kondweretsa.—Yohane 4:24.

Banja laima pakhomo laling’ono la geti ndipo likuyang’ana anthu omwe akudutsa pamsewu wopanikizika

Si zipembedzo zonse zimene zimapezetsa ubwenzi ndi Mulungu. Yesu, amene ndiye bwenzi lenileni lapamtima la Mulungu, analankhula za njira ziŵiri. Njira ina n’njotakata ndipo ili ndi anthu ambiri. Njira imeneyo imatsogolera ku chiwonongeko. Njira inayo n’njopapatiza ndipo ili ndi anthu oyendamo oŵerengeka. Njira imeneyo imatsogolera ku moyo wosatha. Izi zimatanthauza kuti ngati mufuna kukhala paubwenzi ndi Mulungu, muyenera kuphunzira njira yolondola yom’lambirira.—Mateyu 7:13, 14.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena