Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • be phunziro 43 tsamba 234-tsamba 235 ndime 3
  • Kukamba Mfundo za M’nkhani Imene Mwapatsidwa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kukamba Mfundo za M’nkhani Imene Mwapatsidwa
  • Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
  • Nkhani Yofanana
  • Kukonzekera Nkhani ya Wophunzira mu Sukulu
    Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
  • Phindu la Kukonzekera
    Buku Lolangiza la Sukulu ya Utumiki Wateokalase
  • Kukonzekera Nkhani Zokambira Mpingo
    Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
  • Kukonza Autilaini
    Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
Onani Zambiri
Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
be phunziro 43 tsamba 234-tsamba 235 ndime 3

PHUNZIRO 43

Kukamba Mfundo za M’nkhani Imene Mwapatsidwa

Kodi muyenera kuchita motani?

Kambani mfundo zogwirizana ndi nkhani imene mwapatsidwa, ndipo ngati mwapatsidwa gwero lotengako mfundo zanu, malemba ndi mfundo zazikulu zichokerenso mmenemo.

N’chifukwa chiyani kuli kofunikira?

Ngati tikamba mfundo za m’nkhani imene tapatsidwa, timalemekeza dongosolo logaŵira chakudya chauzimu limene gulu la kapolo wokhulupirika ndi wanzeru lakhazikitsa.

BAIBULO limafanizira mpingo wachikristu ndi thupi la munthu. Chiwalo chilichonse n’chofunika, koma sikuti ‘zonsezo zili nayo ntchito imodzimodzi’ ayi. Choncho ifenso tiyenera kuchita udindo uliwonse umene tapatsidwa. Zimenezi zimatanthauza kuti tiyenera kumvetsa ndi kukamba bwino nkhani iliyonse imene atipatsa. Tisaone nkhani zina kukhala zosafunikira kwenikweni chifukwa tikuganiza kuti pali nkhani zina zimene zingakhale zokondweretsa kwambiri. (Aroma 12:4-8) Gulu la kapolo wokhulupirika ndi wanzeru lili ndi udindo wogaŵira chakudya chauzimu “panthaŵi yake.” (Mat. 24:45) Pamene tigwiritsa ntchito luso lathu kukamba nkhani malinga ndi malangizo amene talandira, timasonyeza kuyamikira dongosolo limenelo. Zimenezi zimathandiza kuti mpingo wonse uziyenda bwino.

Zoyenera Kukamba. Ngati mwapatsidwa nkhani m’sukulu, onetsetsani kuti mukukamba mfundo za nkhani imeneyo osatinso zina zosiyana. Nthaŵi zambiri, adzakuuzani nkhani yotengamo mfundo zanu. Ngati sanakuuzeni nkhani yosindikizidwa yoti mutengemo mfundo zokambira nkhani yanu, sankhani nokha gwero lopezako mfundozo. Komabe, pamene mukukonzekera nkhani yanu, tsimikizirani kuti mfundo zanu zonse zikugwirizana ndi nkhani imene akupatsani. Posankha zoyenera kulankhula, ganiziraninso omvera anu.

Ŵerengani mosamala nkhani zina zimene alozako, ndi kupenda malemba opezeka mmenemo. Ndiyeno onani mmene mungazifotokozere kuti mupindulitse omvera. Sankhani mfundo zazikulu ziŵiri kapena zitatu m’nkhani yosindikizidwayo zimene mungagwiritse ntchito m’nkhani yanu. Mofananamo, sankhani pankhani imene mwapatsidwayo malemba amene mungaŵerenge ndi kuwafotokoza.

Kodi muyenera kufotokoza mfundo zochuluka motani? Zokhazo zimene mungafotokoze mogwira mtima. Musanyalanyaze luso la kuphunzitsa kungoti mufotokoze mfundo zambiri. Ngati mfundo zina sizikugwirizana ndi cholinga cha nkhani yanu, tsatirani mfundo zimene zingakuthandizeni kukwaniritsa cholingacho. Pankhani imene mwapatsidwa, fotokozani mfundo zimene omvera angaphunzirepo kanthu ndi kupindula nazo. Cholinga chanu pa mfundo yolangizira imeneyi, sindicho kuona kuchuluka kwa mfundo zimene mungafotokoze, koma kukamba zimene mwapatsidwa ngati maziko a nkhani yanu.

Nkhani yanu isangokhala chidule cha nkhani yosindikizidwa imene akulozerani kuti mutengeko mfundo zanu. Konzekerani kufotokoza mfundo zina mwatsatanetsatane, perekani mafanizo, ndipo ngati n’kotheka perekani chitsanzo cha mmene tingazigwiritsire ntchito. Gwiritsani ntchito mfundo zina pofotokoza mfundo zofunika kwambiri zimene mwapatsidwa m’malo mozisiya n’kutenga za kwina.

Abale okhala ndi luso lophunzitsa m’kupita kwa nthaŵi angapatsidwe mwayi wophunzitsa pa Msonkhano wa Utumiki. Iwo amazindikira kufunika kolankhula mfundo zoperekedwa m’malo motenga za kwina. Mofananamo, abale omwe amakamba nkhani za onse amapatsidwa autilaini yoti atsatire. Maautilaini ameneŵa amapereka ufulu wosankhapo mfundo, komanso amasonyeza bwino lomwe mfundo zazikulu zofunika kufotokoza, zifukwa zake, ndi malemba opereka maziko a nkhaniyo. Kudziŵa kuphunzitsa mwa kugwiritsa ntchito mfundo zochokera m’nkhani imene mwapatsidwa monga maziko a nkhani yanu ndi mbali yofunika kwambiri yokonzekera mwayi wodzakamba nkhani zokulirapo.

Kuphunzira luso limeneli kungakuthandizeninso kuchititsa maphunziro a Baibulo opita patsogolo. Mungaphunzire kuika maganizo pa mfundo zophunziridwa m’malo mochoka pa nkhaniyo ndi kuyamba kufotokoza zinthu zina zimene zingakhale zosangalatsa koma zosathandiza kwenikweni kumveketsa nkhani yanu. Komanso, ngati mwamvetsa bwino cholinga cha phunziroli, simudzangomamatira pa mfundozo moti n’kulephera kuwonjezapo malongosoledwe ena amene angathandize wophunzirayo.

MMENE MUNGACHITIRE ZIMENEZO

  • Kambani mfundo zokhudzana mwachindunji ndi nkhani imene mwapatsidwa.

  • Ngati mwapatsidwa nkhani yosindikiza ngati gwero la nkhani yoti mukambe, sankhani mfundo zazikulu ndi malemba ofunika kwambiri kuchokera m’nkhani yosindikizayo m’malo mokatenga za kwina.

ZOCHITA: Pamasiku atatu amene mwaŵerenga lemba la tsiku, lembani mzera wozungulira liwu kapena mawu osonyeza nkhani yomwe akufotokoza. Lembani mzera kunsi kwa ndemanga imodzi yachidule kapena ziŵiri zokhudzana mwachindunji ndi nkhaniyo. Ndiyeno m’mawu anuanu, thirirani ndemanga pa nkhaniyo mwa kugwiritsa ntchito lemba ndi mfundo zomwe mwachongazo.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena