Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • bh tsamba 199-tsamba 201 ndime 4
  • Yesu Ndi Mesiya Amene Mulungu Ananeneratu Kuti Adzabwera

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yesu Ndi Mesiya Amene Mulungu Ananeneratu Kuti Adzabwera
  • Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni?
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Maulosi Onena za Mesiya Amatsimikizira Kuti Yesu Analidi Mesiya?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Baibulo Linaneneratu za Mesiya
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Anthu Ankayembekezera Mesiya
    Nsanja ya Olonda—2011
  • Mesiya
    Galamukani!—2015
Onani Zambiri
Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni?
bh tsamba 199-tsamba 201 ndime 4

ZAKUMAPETO

Yesu Ndi Mesiya Amene Mulungu Ananeneratu Kuti Adzabwera

POFUNA kutithandiza kuti tidzathe kuzindikira Mesiya, Yehova Mulungu anauzira aneneri ambiri kuti alembe nkhani zokhudza kubadwa kwa Mpulumutsiyu, utumiki wake, ndiponso imfa yake. Maulosi onsewa anakwaniritsidwa pa Yesu Khristu. N’zochititsa chidwi kuona mmene maulosiwa anafotokozera zinthu motsatirika komanso molondola. Kuti timvetse mfundo imeneyi, tiyeni tikambirane maulosi angapo okhudza kubadwa kwa Mesiya ndiponso zinthu zimene zinachitika ali mwana.

Mneneri Yesaya ananeneratu kuti Mesiya adzabadwira m’banja la Mfumu Davide. (Yesaya 9:7) Yesu anabadwiradi m’banja la Davide.—Mateyu 1:1, 6-17.

Mneneri winanso wa Mulungu, dzina lake Mika, ananeneratu kuti mwana ameneyu akadzakula adzakhala mfumu komanso kuti adzabadwira ku “Betelehemu Efurata.” (Mika 5:2) Pa nthawi imene Yesu anabadwa, ku Isiraeli kunali mizinda iwiri imene inkadziwika ndi dzina lakuti Betelehemu. Mzinda umodzi unali kufupi ndi ku Nazareti, pomwe wina unali kufupi ndi Yerusalemu ku Yuda. Mzinda wa Betelehemu wakufupi ndi Yerusalemu poyamba unkatchulidwa kuti Efurata ndipo kumeneku ndi komwe Yesu anabadwira mogwirizana ndi mmene ulosi unanenera.—Mateyu 2:1.

Ulosi wina unaneneratu kuti Mwana wa Mulungu adzaitanidwa kuti “atuluke mu Iguputo.” Yesu ali mwana makolo ake anapita naye ku Iguputo. Iwo anabwerera naye kwawo pambuyo pa imfa ya Herode ndipo kumeneku kunali kukwaniritsidwa kwa ulosiwu.—Hoseya 11:1; Mateyu 2:15.

Pa tchati chimene chili patsamba 200, malemba amene ali pansi pa mutu wakuti “Ulosi” akufotokoza zinthu zosiyanasiyana zokhudza Mesiya. Yerekezetsani zimene malemba amenewa akunena ndi zomwe zili m’malemba omwe ali pansi pa mutu wakuti “kukwaniritsidwa kwake.” Kuchita zimenezi kungawonjezere zifukwa zina zokuchititsani kukhulupirira kuti Mawu a Mulungu ndi oona.

Mukamawerenga malembawa muyenera kukumbukira kuti malemba amene ali ndi ulosiwo analembedwa zaka zambirimbiri Yesu asanabadwe. Yesu ananena kuti: “Zonse zokhudza ine zolembedwa m’chilamulo cha Mose, m’Zolemba za aneneri ndi m’Masalimo ziyenera kukwaniritsidwa.” (Luka 24:44) Ndipo mukaona m’Baibulo lanu mungatsimikizire kuti maulosi onsewa anakwaniritsidwadi.

MAULOSI ONENA ZA MESIYA

CHOCHITIKA

ULOSI

KUKWANIRITSIDWA KWAKE

Adzabadwira m’fuko la Yuda

Genesis 49:10

Luka 3:23-33

Adzabadwa kwa namwali

Yesaya 7:14

Mateyu 1:18-25

Adzabadwira m’banja la Mfumu Davide

Yesaya 9:7

Mateyu 1:1, 6-17

Yehova adzalengeza yekha kuti ndi mwana wake

Salimo 2:7

Mateyu 3:17

Anthu ambiri sadzamukhupirira

Yesaya 53:1

Yohane 12:37, 38

Adzalowa mu Yerusalemu atakwera pa bulu

Zekariya 9:9

Mateyu 21:1-9

Mnzake adzamupereka kwa adani

Salimo 41:9

Yohane 13:18, 21-30

Munthu wom’perekayo adzalandira ndalama 30 zasiliva

Zekariya 11:12

Mateyu 26:14-16

Sadzayankha chilichonse kwa anthu omuimba mlandu

Yesaya 53:7

Mateyu 27:11-14

Adzachita maere pogawana zovala zake

Salimo 22:18

Mateyu 27:35

Adzanyozedwa ali pamtengo wozunzikirapo

Salimo 22:7, 8

Mateyu 27:39-43

Mafupa ake sadzathyoledwa

Salimo 34:20

Yohane 19:33, 36

Adzaikidwa m’manda limodzi ndi anthu olemera

Yesaya 53:9

Mateyu 27:57-60

Adzaukitsidwa thupi lake lisanawonongeke

Salimo 16:10

Machitidwe 2:24, 27

Adzakwezedwa kudzanja lamanja la Mulungu

Salimo 110:1

Machitidwe 7:56

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena