Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • lfb phunziro 42 tsamba 102-tsamba 103 ndime 3
  • Yonatani Anali Wolimba Mtima Komanso Wokhulupirika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yonatani Anali Wolimba Mtima Komanso Wokhulupirika
  • Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Jonatani Anachita Zinthu Mothandizidwa ndi Mulungu
    Nsanja ya Olonda—2007
  • Ogwirizana Pansi pa Mbendera ya Chikondi
    Nsanja ya Olonda—1989
  • Muzikhala Okhulupirika kwa Yehova
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2016
  • Pitirizani Kusonyezana Chikondi Chenicheni
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2021
Onani Zambiri
Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
lfb phunziro 42 tsamba 102-tsamba 103 ndime 3
Yonatani ndi mtumiki wake amene ankamunyamulira zida

MUTU 42

Yonatani Anali Wolimba Mtima Komanso Wokhulupirika

Mwana wamkulu wa Mfumu Sauli anali Yonatani ndipo anali msilikali wolimba mtima. Davide ananena kuti Yonatani ankathamanga kuposa chiwombankhanga ndipo anali wamphamvu kuposa mkango. Tsiku lina, Yonatani anaona asilikali 20 a Afilisiti ali paphiri. Iye anauza mtumiki wake amene ankamunyamulira zida kuti: ‘Awotu tikhoza kuwagonjetsa. Tiye tione ngati Yehova angatipatse chizindikiro. Akatiuza kuti tipite ndiye kuti ndi nthawi yabwino ndipo tikawagonjetsa.’ Nthawi yomweyo Afilisitiwo anafuula kuti: ‘Bwerani tikukhaulitseni!’ Yonatani ndi mtumiki wakeyo anakweradi phirilo ndipo anakawagonjetsa.

Yonatani akupatsa Davide zinthu zake zina

Popeza Yonatani anali mwana woyamba, anali woyenera kudzalowa ufumu wa Sauli. Koma iye ankadziwa kuti Yehova anasankha Davide ndipo sankamuchitira nsanje. Yonatani ndi Davide ankagwirizana kwambiri ndipo analonjezana kuti azitetezana. Yonatani anapatsa Davide zovala zake zankhondo, lupanga, uta ndi lamba posonyeza kuti ndi mnzake wapamtima.

Pa nthawi ina, Davide akuthawa Sauli, mnzakeyu anapita kukamuuza kuti: ‘Limba mtima ndipo usaope chilichonse. Yehova wakusankha kuti ukhale mfumu. Ngakhale bambo anga akudziwa zimenezi.’ Kodi iweyo ungafune kukhala ndi mnzako wabwino ngati Yonatani?

Yonatani ankaika moyo wake pangozi pofuna kuthandiza Davide. Iye ankadziwa zoti Mfumu Sauli akufuna kupha Davide ndiye anauza bambo akewo kuti: ‘Bambo mukudziwa kuti mukulakwa? Kodi Davide wakulakwirani chiyani kuti mumuphe?’ Koma Sauli anamukwiyira kwambiri Yonatani. Patapita zaka, Sauli ndi Yonatani anafera kunkhondo.

Yonatani atafa, Davide anafufuza mwana wake dzina lake Mefiboseti. Atamupeza anamuuza kuti: ‘Bambo ako tinkagwirizana kwambiri choncho ndikusamalira kwa moyo wako wonse. Uzikhala m’nyumba mwanga ndipo tizidyera limodzi.’ Apatu Davide anasonyeza kuti sanaiwale Yonatani.

“Muzikondana mofanana ndi mmene ine ndimakukonderani. Palibe amene ali ndi chikondi chachikulu kuposa cha munthu amene wapereka moyo wake chifukwa cha anzake.”​—Yohane 15:12, 13

Mafunso: Kodi Yonatani anasonyeza bwanji kuti anali wolimba mtima? Nanga anasonyezanso bwanji kuti anali wokhulupirika?

1 Samueli 14:1-23; 18:1-4; 19:1-6; 20:32-42; 23:16-18; 31:1-7; 2 Samueli 1:23; 9:1-13

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena