Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • lfb phunziro 100 tsamba 232-tsamba 233 ndime 2
  • Paulo, Sila ndi Timoteyo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Paulo, Sila ndi Timoteyo
  • Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Timoteyo Anali Wokonzeka Komanso Wofunitsitsa Kutumikira
    Nsanja ya Olonda—2008
  • Timoteyo Ankafuna Kuthandiza Anthu
    Phunzitsani Ana Anu
  • Timoteo—‘Mwana Weniweni m’Chikhulupiriro’
    Nsanja ya Olonda—1999
  • “Mwana Wanga Wokondedwa Ndi Wokhulupirika Mwa Ambuye”
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
Onani Zambiri
Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
lfb phunziro 100 tsamba 232-tsamba 233 ndime 2
Paulo, Sila ndi Timoteyo

MUTU 100

Paulo ndi Timoteyo

Yunike, Loisi komanso Timoteyo ali wamng’ono

Timoteyo anali m’bale wachinyamata mumpingo wa ku Lusitara. Bambo ake anali Mgiriki ndipo mayi ake anali Myuda. Timoteyo anaphunzira Mawu a Mulungu kuyambira ali wakhanda ndipo amene ankamuphunzitsa ndi mayi ake, a Yunike ndi agogo ake, a Loisi.

Paulo atafika ku Lusitara pa ulendo wake wachiwiri, anazindikira kuti Timoteyo amakonda kwambiri abale ndipo ali ndi mtima wofuna kuwathandiza. Choncho Paulo anapempha Timoteyo kuti aziyenda naye. Paulo anaphunzitsa Timoteyo kulalikira komanso kuphunzitsa uthenga wabwino mwaluso.

Mzimu woyera unkathandiza Paulo ndi Timoteyo kulikonse kumene ankapita. Tsiku lina usiku, Paulo anaona m’masomphenya munthu akumuuza kuti apite ku Makedoniya kukawathandiza. Choncho Paulo, Timoteyo, Sila ndi anthu ena anapita kukalalikira ku Makedoniya ndipo anakhazikitsa mipingo.

Atafika mumzinda wa Tesalonika, anthu ambiri anakhala Akhristu. Koma Ayuda ena ankachitira nsanje Paulo ndi anzakewo. Iwo anakopa gulu la anthu n’kutenga Paulo ndi anzakewo kupita nawo kwa olamulira a mzinda. Anthuwo ankafuula kuti: ‘Anthu awa ndi adani a boma la Roma!’ Apa moyo wa Paulo ndi Timoteyo unali pa ngozi choncho kutangoda iwo anathawira ku Bereya.

Anthu a ku Bereya anali ofunitsitsa kumvetsera uthenga wabwino ndipo Agiriki ndi Ayuda omwe, anakhala okhulupirira. Koma Ayuda amene anachokera ku Tesalonika atabwera anayambitsa chipolowe, ndiye Paulo anachoka kupita ku Atene. Timoteyo ndi Sila anatsala ku Bereya komweko kuti azilimbikitsa abale. Patapita nthawi, Paulo anatumiza Timoteyo ku Tesalonika kuti akalimbikitse abale kumeneko, omwe ankazunzidwa kwambiri. Kenako anamutumizanso kumipingo ina kuti akalimbikitse abale ndi alongo.

Mtumwi Paulo wamangidwa koma akuuza Timoteyo zoti alembe m’kalata

Paulo anauza Timoteyo kuti: ‘Amene akufuna kutumikira Yehova adzazunzidwa.’ Timoteyo anazunzidwa ndiponso kutsekeredwa m’ndende chifukwa chotumikira Mulungu. Iye ankaona kuti umenewu unali mwayi wake wosonyeza kuti ndi wokhulupirika kwa Yehova.

Paulo anauza Akhristu a ku Filipi kuti: ‘Ndakutumizirani Timoteyo kuti adzakuphunzitseni zoyenera kuchita potumikira Mulungu komanso polalikira.’ Paulo anachita zimenezi chifukwa chakuti Timoteyo anali wodalirika. Paulo ndi Timoteyo ankagwirizana kwambiri ndipo anatumikira Mulungu limodzi kwa zaka zambiri.

“Ndilibe wina amene ali ndi mtima ngati wake, amene angasamaliredi moona mtima zosowa zanu. Anthu ena onse akungoganizira zofuna zawo zokha, osati za Yesu Khristu.”—Afilipi 2:20, 21

Mafunso: Kodi Timoteyo anali ndani? N’chifukwa chiyani Paulo ndi Timoteyo ankagwirizana kwambiri?

Machitidwe 16:1-12; 17:1-15; Afilipi 2:19-22; 2 Timoteyo 1:1-5; 3:12, 14, 15; Aheberi 13:23

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena