Mawu Oyamba Gawo 3
Baibulo limanena kuti Chigumula chitatha, panali anthu ena omwe ankatumikira Yehova. Ena mwa anthuwa anali Abulahamu amene ankadziwika kuti anali mnzake wa Yehova. N’chifukwa chiyani Abulahamu ankatchedwa mnzake wa Yehova? Ngati ndinu kholo, thandizani mwana wanu kudziwa kuti Yehova amamukonda kwambiri ndipo amafunitsitsa kumuthandiza. Mofanana ndi Abulahamu komanso anthu ena okhulupirika monga Loti ndi Yakobo, tingathe kupempha Yehova kuti atithandize. Komanso tizikhulupirira kuti Yehova adzachita chilichonse chimene wanena.