Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • lvs tsamba 3
  • Kalata Yochokera ku Bungwe Lolamulira

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kalata Yochokera ku Bungwe Lolamulira
  • Kodi Mungatani Kuti Mulungu Azikukondani?
  • Werengani mu ‘Mulungu Apitirize Kukukondani’
  • Nkhani Yofanana
  • Chikondi Cha Mulungu Sichimatha
    Kodi Mungatani Kuti Mulungu Azikukondani?
  • Zimene Mungachite Kuti Mulungu Apitirize Kukukondani
    Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni?
  • Musalole Kuti Chikondi Chanu Chizirale
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2017
  • Zimene “Kukonda Mulungu Kumatanthauza”
    Kodi Mungatani Kuti ‘Mulungu Apitirize Kukukondani’?
Onani Zambiri
Kodi Mungatani Kuti Mulungu Azikukondani?
lvs tsamba 3

Kalata Yochokera ku Bungwe Lolamulira

Kwa anthu amene amakonda Yehova Mulungu ndiponso Baibulo:

Yesu ananena kuti: “Mudzadziwa choonadi, ndipo choonadi chidzakumasulani.” (Yohane 8:32) Takumbukirani mmene munamvera mutangophunzira kumene choonadi kuchokera m’Baibulo. Munasangalala kudziwa kuti n’zotheka kuphunzira choonadi ngakhale kuti tikukhala m’dziko lodzadza ndi bodza.​—2 Timoteyo 3:1.

Yehova Mulungu amafuna kuti tidziwe choonadi. Ndipo timafuna kuuza ena za choonadichi chifukwa chakuti timawakonda. Koma pali zambiri zimene tiyenera kuchita potumikira Mulungu. Tiyenera kuyesetsa kumakhala monga Akhristu chifukwa choti timalemekeza kwambiri mfundo za Yehova. Yesu anafotokoza njira imodzi yofunika yomwe tingamusonyezere Mulungu kuti timamukonda. Iye ananena kuti: “Mukasunga malamulo anga, mudzakhalabe m’chikondi changa, monga mmene ine ndasungira malamulo a Atate ndi kukhalabe m’chikondi chake.”​—Yohane 15:10.

Yesu amakonda kwambiri Atate ake ndipo amachita chilichonse chimene amamuuza kuti achite. Ngati titamatsanzira Yesu pa moyo wathu, Yehova adzatikonda ndipo tidzakhala wosangalala. Ndipotu paja Yesu ananena kuti: “Ngati zimenezi mukuzidziwa, ndinu odala mukamazichita.”​—Yohane 13:17.

Tikukhulupirira kuti bukuli likuthandizani kuti muzikhala mogwirizana ndi choonadi cha m’Baibulo ndiponso kuti mukhale pa ubwenzi ndi Yehova. Pemphero lathu ndi lakuti mupitirize kukulitsa chikondi chanu pa Yehova komanso kupitiriza kuchita zimene zingachititse Mulungu kukukondani kuti ‘mudzalandire moyo wosatha.’​—Yuda 21.

Bungwe Lolamulira la Mboni za Yehova

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena