Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • lff phunziro 2
  • Baibulo Limatithandiza Kuti Tikhale Ndi Chiyembekezo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Baibulo Limatithandiza Kuti Tikhale Ndi Chiyembekezo
  • Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • FUFUZANI MOZAMA
  • ZOMWE TAPHUNZIRA
  • ONANI ZINANSO
  • Baibulo Limatithandiza Kukhala Ndi Chiyembekezo
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Yambani Kuphunzira Baibulo
  • Tiziyembekezera Kuti Zinthu Zidzakhala Bwino M’tsogolo
    Nkhani Zina
  • Yambani Chaka cha 2023 Muli Ndi Chiyembekezo—Kodi Baibulo Limanena Zotani?
    Nkhani Zina
  • Mungakhale Ndi Chiyembekezo Chabwino mu 2024—Kodi Baibulo Limanena Zotani?
    Nkhani Zina
Onani Zambiri
Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
lff phunziro 2
Phunziro 2. Dzuwa likutuluka pamwamba pa munda waukulu wa tirigu.

PHUNZIRO 02

Baibulo Limatithandiza Kuti Tikhale Ndi Chiyembekezo

Losindikizidwa
Losindikizidwa
Losindikizidwa

Anthu padziko lonse amakumana ndi mavuto amene amawachititsa kuti azikhumudwa, azida nkhawa komanso azimva kupweteka. Kodi inunso munakumanapo ndi vuto limene linakuchititsani kumva chonchi? Mwina panopa mukudwala kapena munthu amene munkamukonda anamwalira. Mwina mukudzifunsa kuti, ‘Koma zinthu zidzakhalanso bwino?’ Baibulo limayankha mogwira mtima funso limeneli.

1. Kodi Baibulo limatithandiza bwanji kukhala ndi chiyembekezo?

Baibulo limafotokoza chifukwa chake padzikoli pali mavuto ochuluka chonchi, komanso limatiuza uthenga wabwino wakuti posachedwapa mavuto onsewa atha. Zimene Baibulo limalonjeza zingatithandize kukhala ndi “tsogolo labwino ndi chiyembekezo chabwino.” (Werengani Yeremiya 29:11, 12.) Malonjezo amenewa amatithandiza kuti tizitha kupirira mavuto, tiziona zinthu moyenera ndiponso amatitsimikizira kuti tidzakhala osangalala mpaka kalekale.

2. Kodi Baibulo limafotokoza kuti m’tsogolomu mudzachitika zotani?

Baibulo limanena kuti m’tsogolomu “imfa sidzakhalaponso. Sipadzakhalanso kulira, kubuula kapena kupweteka.” (Werengani Chivumbulutso 21:4.) Mavuto amene tikukumana nawo masiku ano monga umphawi, kupanda chilungamo, matenda komanso imfa sadzakhalaponso. Baibulo limalonjeza kuti anthu adzakhala ndi moyo wosatha m’Paradaiso padziko lapansi.

3. Kodi inuyo mungatani kuti muzikhulupirira kuti zimene Baibulo limalonjeza zidzachitikadi?

Anthu ambiri amafuna zinthu zabwino zitachitika, koma sakhulupirira ndi mtima wonse kuti zidzachitikadi. Koma zimene Baibulo limalonjeza zidzachitika ndithu. Tingakhulupirire kwambiri zimene Baibulo limanena ngati tikuyesetsa ‘kufufuza Malemba mosamala.’ (Machitidwe 17:11) Mukamaphunzira Baibulo, mudziwa zimene limanena zokhudza zimene zidzachitike m’tsogolo. Ndiye zili ndi inu kuzikhulupirira kapena ayi.

FUFUZANI MOZAMA

Fufuzani zinthu zina zimene Baibulo limalonjeza kuti zidzachitika m’tsogolo ndipo onani mmene chiyembekezo chotchulidwa m’Baibulo chikuthandizira anthu masiku ano.

Zithunzi: Zithunzi zosonyeza mmene moyo ulili masiku ano tikayerekezera ndi mmene udzakhalire m’tsogolomu. Chithunzi chilichonse chabwerezedwa pansipa.

4. Baibulo limatilonjeza moyo wosatha komanso wopanda mavuto

Taonani malonjezo otsatirawa amene amapezeka m’Baibulo. Kodi ndi malonjezo ati amene akusangalatsani kwambiri? Nanga n’chifukwa chiyani mukutero?

Werengani malemba amene ali pa lonjezo lililonse, kenako yankhani mafunso awa:

  • Kodi malemba amenewa akukupangitsani kuyembekezera zinthu zabwino? Nanga angathandizenso anthu a m’banja lanu ndi anzanu kuyembekezera zinthu zabwino?

Yerekezerani kuti muli m’dziko lomwe

PALIBE ALIYENSE AMENE . . .

ALIYENSE ALI NDI MWAYI . . .

  • akumva kupweteka, kuvutika ndi ukalamba kapena kumwalira.​—Yesaya 25:8.

  • woona anthu amene anamwalira akuukitsidwa padziko lapansi.​—Yohane 5:28, 29.

  • akudwala kapena kulumala.​—Yesaya 33:24; 35:5, 6.

  • wokhala ndi thanzi labwino komanso mphamvu.​—Yobu 33:25.

  • akuchitiridwa zinthu zopanda chilungamo.​—Yesaya 32:​16, 17.

  • wokhala ndi chakudya chokwanira, nyumba yabwino komanso ntchito yosangalatsa.​—Salimo 72:16; Yesaya 65:21, 22.

  • akuvutika ndi nkhondo.​—Salimo 46:9.

  • wokhala mwamtendere mpaka kalekale.​—Salimo 37:11.

  • akuvutika maganizo kapena kukumbukira mavuto.​—Yesaya 65:17.

  • wokhala ndi moyo wosatha m’dziko labwino kwambiri.​—Salimo 37:29.

Mnyamata yemwe ankadwala pano ali bwinobwino ndipo akuhaga mayi ake. Bambo amene anali wokalamba pano ndi wachinyamata ndipo akuyendetsa wilibala yomwe muli masamba. Ana amene ankavutika ndi njala ndiponso kugwira ntchito mokakamizidwa tsopano akubzala mbewu m’munda komanso akusewera mpira. Mzimayi amene anakhumata ndi mavuto tsopano waimirira ndipo akumwetulira.

5. Zimene Baibulo likulonjeza zingakuthandizeni panopa

Anthu ambiri amakhumudwa kapenanso kukwiya akaona mavuto amene ali m’dzikoli. Anthu ena amayesetsa kumenyera ufulu kuti zinthu zisinthe. Onani mmene malonjezo a m’Baibulo akuti zinthu zidzasintha akuthandizira anthu masiku ano. Onerani VIDIYO, kenako mukambirane mafunso otsatirawa.

VIDIYO: Ndinkafunitsitsa Kuthana ndi Kupanda Chilungamo (4:07)

Zithunzi: Zithunzi za muvidiyo yakuti ‘Ndinkafunitsitsa Kuthana ndi Kupanda Chilungamo.’ 1. Rafika ali mtsikana ankakolola thonje ndi anthu amtundu wake. 2. Rafika akusangalala kwambiri kuona anthu amitundu yosiyanasiyana akuchita zinthu mogwirizana atapita koyamba kumsonkhano wachigawo wa Mboni za Yehova.
  • Muvidiyoyi, kodi ndi zinthu ziti zopanda chilungamo zimene zinkamupweteka kwambiri Rafika?

  • Ngakhale kuti zinthu zopanda chilungamozo sizinathe, kodi Baibulo linamuthandiza bwanji?

Zimene Baibulo limatilonjeza zimatithandiza kuti tiziyembekezera kuti m’tsogolo zinthu zidzakhala bwino ndipo timasiya kukhumudwa n’kumapirira mavuto athu bwinobwino. Werengani Miyambo 17:22 ndi Aroma 12:12, kenako mukambirane mafunso awa:

  • Kodi mukuganiza kuti uthenga wa chiyembekezo wopezeka m’Baibulo ungakuthandizeni pa moyo wanu masiku ano? N’chifukwa chiyani mukutero?

ANTHU ENA AMANENA KUTI: “Zimene Baibulo limalonjeza ndi zabwino kwambiri, koma sizingatheke.”

  • N’chifukwa chiyani muyenera kufufuza umboni wakuti zimene Baibulo limalonjeza zidzachitikadi?

ZOMWE TAPHUNZIRA

Baibulo limatithandiza kukhala ndi chiyembekezo ndipo limatilonjeza kuti tidzasangalala m’tsogolo. Zimenezi zimatithandiza kuti tipirire mavuto athu panopa.

Kubwereza

  • N’chifukwa chiyani anthu akufunika kudziwa zimene Mulungu akutilonjeza?

  • Kodi Baibulo limati m’tsogolo mudzachitika zotani?

  • Kodi kuyembekezera kuti m’tsogolo zinthu zidzakhala bwino kungatithandize bwanji masiku ano?

Zoti Muchite

ONANI ZINANSO

Onani mmene kuyembekezera zinthu zabwino kungakuthandizireni mukakhala pa mavuto.

“Kodi Chiyembekezo Mungachipeze Kuti?” (Galamukani!, May 8, 2004)

Onani mmene kuyembekezera zinthu zabwino za m’tsogolo kungathandizire anthu amene akudwala.

“Kodi Baibulo Lingandithandize Kupirira Matenda?” (Nkhani yapawebusaiti)

Mukamaonera nyimboyi, muziganizira mmene inuyo ndi banja lanu mudzasangalalire ndi moyo m’Paradaiso amene Baibulo linalonjeza.

Ganizira Nthawiyo (3:37)

Onani mmene munthu wina yemwe ankamenyera ufulu wa anthu ndi zinyama anasinthira moyo wake atangophunzira zimene Baibulo limalonjeza zokhudza m’tsogolo.

“Panopa Ndilibenso Maganizo Ofuna Kusintha Zinthu M’dzikoli” (Nsanja ya Olonda, July 1, 2013)

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena