Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w90 7/15 tsamba 6
  • Chifukwa Chakuti Anapemphera

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Chifukwa Chakuti Anapemphera
  • Nsanja ya Olonda​—1990
  • Nkhani Yofanana
  • N’chifukwa Chiyani Tiyenera Kupemphera Kosaleka?
    Nsanja ya Olonda—2003
  • 5 Kodi Tiyenera Kupemphera Pamalo Ati, Nanga Nthawi Yanji?
    Nsanja ya Olonda—2010
  • Kwezani Manja Okhulupirika m’Pemphero
    Nsanja ya Olonda—1999
  • Yesu Atiphunzitsa Kupemphera
    Phunzirani kwa Mphunzitsi Waluso
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda​—1990
w90 7/15 tsamba 6

Chifukwa Chakuti Anapemphera

PA 1 Atesalonika 5:17, 18, mtumwi Paulo adaati: “Pempherani kosaleka; M’zonse yamikani; pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu cha kwa inu, mwa Kristu Yesu.” Komabe, kodi nthaŵi zina mumazengereza kupereka chiyamiko pamene mukusangalala ndi chakudya m’malo apoyera, onga ngati kantini? Polingalira za chenjezo la Yesu lotsutsa pemphero lodziwonetsera, mwachiwonekere munthu angafune kupeŵa kukokera chisamaliro cha ena mosayenera kwa iyemwini. (Mateyu 6:5, 6) Komabe, pemphero loperekedwa mwanzeru lingakope ena moyanja.

Ichi chinali chokumana nacho cha minisitala wina wachichepere wotumikira pa Beteli ya Brooklyn, malikulu a padziko lonse a Mboni za Yehova. Iye ankafisula pakantini, akumakonzekera kupita kumpingo wake kukakumana ndi kagulu kamene kanali kudzagaŵana m’ntchito yolalikira Ufumu. Pamene chakudya chakufisula chinadza, anapereka pemphero mwanjira yake yanthaŵi zonse. Atatsegula maso, anatukula maso ake ndikuona woperekera wamkazi ali chiriri kumuyang’anitsitsa.

“Ukupemphera eti?” mkaziyo anafunsa. Pamene iye anayankha movomera, mkaziyo anati: “Uyenera kukhala mmodzi wa Mboni za Yehova. Makolo anga alinso. Sindinaphatikizidwedi konse m’chipembedzo chawo, koma ndidziŵa kuti ndiyenera kutero. Mwinamwake ndilembetse Nsanja ya Olonda ndi Galamukani! Kodi ndingawapeze kwa iwe?”

“Panatsala nenene kuti nditsamwitsidwe ndichakudya,” akukumbukira motero mbale wachichepereyo. Chikhalirechobe, anakhoza kumgaŵira masabuskiripishoni aŵiri ndi magazini atsopano aŵiri ndi kupanga makonzedwe a ulendo wobwerera​—zonsezo chifukwa chakuti anapemphera.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena