Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w95 7/15 tsamba 8-9
  • Mboni za Yehova Padziko Lonse—Brazil

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mboni za Yehova Padziko Lonse—Brazil
  • Nsanja ya Olonda—1995
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Kutumikira Kumene Kusoŵa Kuli Kokulira
  • Kugaŵira Mabuku Ofotokoza Baibulo
  • Yehova Akutichinjiriza Ife
    Nsanja ya Olonda—1987
  • Chidaliro Changa mwa Yehova Chinandichirikiza
    Nsanja ya Olonda—1997
  • Khama Lichititsa Kupita Patsogolo
    Nsanja ya Olonda—1995
  • Yehova Anadalitsa Kutsimikiza Mtima Kwanga
    Nsanja ya Olonda​—1990
Nsanja ya Olonda—1995
w95 7/15 tsamba 8-9

Mboni za Yehova Padziko Lonse​—Brazil

BRAZIL ndi dziko lalikulu kwambiri m’mbali zambiri. Mu ukulu ndi chiŵerengero cha anthunso, ndi dziko lalikulu lachisanu padziko lonse. Limatenga pafupifupi theka la dera la South America ndipo lili ndi anthu ambiri kuposa maiko ena a pa kontinentiyo ataphatikizidwa pamodzi. Brazil alinso ndi nkhalango ya mvula yaikulu koposa padziko lonse. M’nkhalango imeneyo mumadutsa mtsinje waukulu koposa pa dziko lapansi​—Amazon.

Brazil alinso dziko lalikulu kwambiri m’lingaliro lina. Chiŵerengero cha ofalitsa ake a uthenga wabwino wa Ufumu wa Mulungu chikuyandikira ku 400,000, ndipo chaka chatha oposa 1,000,000 anafika pa Chikumbutso cha imfa ya Kristu. Chotero dziko limeneli lilidi lapadera kwambiri ponena za ntchito ya kulalikira Ufumu. Zochitika zaposachedwa zikusonyeza mfundo imeneyi.

Kutumikira Kumene Kusoŵa Kuli Kokulira

Antonio ndi mkazi wake anapanga chosankha chovuta cha kusiya achibale awo ndi ntchito yotsimikizirika, ya malipiro abwino ku São Paulo kukatumikira kumene kusoŵa kwa olengeza Ufumu kunali kokulira m’boma la Minas Gerais. Gawo lawo linaphatikizapo mudzi wa antchito apamalo opangira shuga. Tsiku loyamba limene anachitira umboni kumeneko, anayambitsa maphunziro a Baibulo asanu ndi anayi. M’miyezi 18, anali kuchititsa maphunziro oposa 40!

Poyamba, misonkhano inali kuchitidwa pamalo opangira shuga pomwepo. Komabe, ofalitsa atsopanowo anafuna kuona Nyumba Yaufumu yeniyeni. Chotero, anahaya basi yonyamula anthu 75 kumka nawo kumpingo wapafupi. Ndiyeno msonkhano wachigawo unafika; 45 a ophunzira Baibulo atsopanowo anafikapo ndipo anafunsidwa. Mwa ameneŵa, 15 anabatizidwa panthaŵiyo. Zoonadi, panali misozi yachisangalalo!

Mabasi a kampani imodzimodziyo anagwiritsiridwa ntchito pa maulendo ofananawo, ndipo akuluakulu ake anatsitsa mtengo wake. Poyamikira zimenezi, Antonio anapatsa mwini kampaniyo buku lothandizira kuphunzira Baibulo. Iye anavomereza kuyamba kuphunzira Baibulo usiku womwewo ndipo anabatizidwa patapita miyezi yoŵerengeka ya kuphunzira kosamalitsa. Poyamba, mkazi wake anali kutsutsa phunzirolo, koma m’kupita kwa nthaŵi, mkhalidwe wake unasintha. Lerolino nayenso ndi Mboni ya Yehova yobatizidwa.

Mu February 1992 mpingo wokhala ndi ofalitsa okangalika 22 unapangidwa. Podzafika mu 1994 chiŵerengero chimenechi chinawonjezereka kufika pa 42, ndi apainiya 4 okhazikika, kapena alaliki anthaŵi yonse a uthenga wabwino. Chotero, Antonio anati: “Ine ndi mkazi wanga taona kuti ngati ‘tiyesa Yehova,’ monga momwe Malaki 3:10 amanenera, ‘adzatitsanulira mdalitso wakuti adzasoŵeka malo a kuulandirira.’”

Kugaŵira Mabuku Ofotokoza Baibulo

Mwinamwake chifukwa china chimene ntchito yolalikira ikupitira patsogolo kwambiri motero ku Brazil nchakuti Mboni zimagaŵira mabuku ofotokoza Baibulo pa mpata uliwonse. Mwachitsanzo, mpingo wina unalembera ofesi ya nthambi ya Watch Tower Society ukumapempha makope 250 a buku la Mafunso Achichepere Akufunsa​—Mayankho Amene Amathandiza. Nchifukwa ninji anapempha oda yaikulu chotero?

Kalatayo inafotokoza kuti: ‘Sukulu ina m’tauni yasankha kugwiritsira ntchito bukuli kukhala lophunzitsira m’kalasi lina. Chosankha cha akuluakulu a sukuluyo chachitika chifukwa cha umboni wamwamwaŵi umene wachitidwa ndi makolo a ophunzira amene ali Mboni za Yehova ndiponso ndi mmodzi wa oyang’anira sukuluyo. Yehova apitirizetu kudalitsa atumiki ake pamene akupereka malangizo abwino ndi bukuli.’ Inde, ndipo Yehova apitirizetu kudalitsa kupita patsogolo kwabwinoko kwa ntchito yolalikira Ufumu m’dziko limeneli lalikulu la Brazil.

[Bokosi patsamba 8]

ZIŴERENGERO Za Dzikolo

Chaka Chautumiki cha 1994

CHIŴERENGERO CHAPAMWAMBA CHA OCHITIRA UMBONI: 385,099

KUGAŴA: Mboni 1 pa anthu 404

OFIKA PACHIKUMBUTSO: 1,018,210

AVAREJI YA OFALITSA AUPAINIYA: 38,348

AVAREJI YA MAPHUNZIRO A BAIBULO: 461,343

CHIŴERENGERO CHA OBATIZIDWA: 24,634

CHIŴERENGERO CHA MIPINGO: 5,928

OFESI YA NTHAMBI: CESÁRIO LANGE

[Chithunzi patsamba 9]

Galimoto ya chiŵiya chokuza mawu mu São Paulo cha m’ma 1940

[Chithunzi patsamba 9]

Kuchitira umboni mu Botanical Garden ku Rio de Janeiro

[Chithunzi patsamba 9]

Ofesi ya nthambi mu Cesário Lange

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena