Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w97 5/1 tsamba 6
  • ‘Timafuna Anthu Oona Mtima’

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • ‘Timafuna Anthu Oona Mtima’
  • Nsanja ya Olonda—1997
  • Nkhani Yofanana
  • “Osafooka”
    Galamukani!—1991
  • Muzichita Zinthu Zonse Mwachilungamo
    Kodi Mungatani Kuti Mulungu Azikukondani?
  • Muzichita Zinthu Zonse Moona Mtima
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
  • Chitani Zinthu Zonse Moona Mtima
    Kodi Mungatani Kuti ‘Mulungu Apitirize Kukukondani’?
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—1997
w97 5/1 tsamba 6

‘Timafuna Anthu Oona Mtima’

KUONA MTIMA nkovuta kupeza m’dziko lero. Komabe, ndiko chinthu chachikulu chofunika kwa Akristu. Paulo analemba kuti: “Takopeka mtima kuti tili nacho chikumbumtima chokoma m’zonse, pofuna kukhala nao makhalidwe abwino.” (Ahebri 13:18) Izi nzimene anafuna kuchita Wilma, mmodzi wa Mboni za Yehova mu Faenza, ku Italy.

Nyuzipepala ya Il Resto del Carlino inati pamene iye anapeza chikwama mmene munali ndalama zambiri panja pa supamaketi mumzinda wa kwawo, anachipereka kupolisi “mosazengereza” konse kotero kuti akachibwezere kwa mwini wake.

Bwanamkubwa atamva zimenezi, mwamsanga anatumiza kalata yachidule yomuyamikira Wilma. “M’dzina la Mzindawu,” anatero kulemba kwake, “ndikuthokozani kwabasi pakachitidwe kanu kokomako. Mzinda wathu wolemekezekawu wa Faenza umafuna anthu abwino ndi oona mtima.”

Kaya machitidwe abwino adziŵike kapena ayi, nthaŵi zonse tiyenera kuyesa kukhala oona mtima. Monga amalimbikitsira Malemba Oyera, “pakuti tikonzeratu zinthu zokoma, si pamaso pa Ambuye pokha, komanso pamaso pa anthu.”​—2 Akorinto 8:21.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena