Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w03 10/15 tsamba 3
  • Sitingapeŵe Kusankha Zochita

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Sitingapeŵe Kusankha Zochita
  • Nsanja ya Olonda—2003
  • Nkhani Yofanana
  • Muzikhulupirira Yehova Kuti Muzisankha Zochita Mwanzeru
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2017
  • Zosankha Zanu Zizilemekeza Mulungu
    Nsanja ya Olonda—2011
  • Mawu Oyamba
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2024
  • Muzisankha Zochita Mwanzeru
    Nsanja ya Olonda—2013
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2003
w03 10/15 tsamba 3

Sitingapeŵe Kusankha Zochita

NTHAŴI ina Napoleon Bonaparte, mfumu ya ku France ya m’ma 1800, anati: “Palibe chinthu chovuta kwambiri komanso chamtengo wapatali ngati kutha kusankha zochita.” Mungavomereze kuti zimenezi n’zoona, popeza nthaŵi zambiri anthu amasangalala kulamulira moyo wawo. Komanso, anthu aona kuti kusankha zochita n’kovuta.

Kaya n’kovuta kapena ayi, sitingapeŵe kusankha zochita. Tsiku lililonse timafunika kuchita zimenezi. Tikadzuka m’maŵa, timafunika kusankha zoti tivale, zoti tidye pa chakudya cham’maŵa, ndiponso mmene tichitire zinthu zina zambiri patsikulo. Zambiri mwa zosankha zimenezi n’zazing’ono. Kaŵirikaŵiri sitiziganizira mofatsa. Si nthaŵi zambiri zimene timasoŵa tulo chifukwa choganizira ngati tinasankha zinthu zimenezi mwanzeru.

Komano, zina zimene timasankha kuchita zimakhala zazikulu zedi. Achinyamata ambiri m’dziko la masiku ano ayenera kusankha zochita pamoyo wawo. Ayenera kusankha maphunziro amene akufuna ndiponso kuti adzafike nawo pati. M’kupita kwa nthaŵi ambiri a iwo adzafunika kusankha kaya kuloŵa m’banja kapena kupitirizabe kukhala opanda mnzawo wa muukwati. Amene akufuna kuloŵa m’banja ayenera kudzifunsa kuti: ‘Kodi ndine wamkulu ndi wokhwima mokwanira moti n’kuloŵa m’banja? Kodi ndimafuna munthu womanga naye banja wotani, kapena chofunika kwambiri, kodi ndimafunikira munthu womanga naye banja wotani?’ Ndi zinthu zochepa chabe zimene timasankha kuchita zimene zimakhudza kwambiri moyo wathu monga mmene kusankha munthu womanga naye banja kumachitira.

Pa zinthu zofunika kwambiri, n’kofunika kusankha zochita mwanzeru. Izi n’zofunika chifukwa chakuti kusangalala kwathu pamoyo kumadalira kwambiri kuchita zimenezi. Anthu ena amaona kuti akhoza kusankha bwino zochita zoterozo ndipo amakana anthu kuwathandiza. Kodi zimenezo ndi nzeru? Tiyeni tione.

[Mawu a Chithunzi patsamba 3]

Napoleon: From the book The Pictorial History of the World

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena