Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w13 12/1 tsamba 16
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Nsanja ya Olonda—2013
  • Nkhani Yofanana
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
    Nsanja ya Olonda—2013
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
    Nsanja ya Olonda—2014
  • Kodi Mulungu Adzakhazikitsa Boma Lolamulira Dziko Lonse Lapansi?
    Nsanja ya Olonda—2012
  • Zokhudza Ufumu wa Mulungu
    Nsanja ya Olonda—2008
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2013
w13 12/1 tsamba 16
[Chithunzi patsamba 16]

KUYANKHA MAFUNSO A M’BAIBULO

Kodi cholinga cha kubweranso kwa Yesu n’chiyani?

Yesu asanakwere kumwamba mu 33 C.E., analonjeza otsatira ake kuti adzabweranso. Anadziyerekezera ndi munthu wa m’banja lachifumu amene anapita kudziko lakutali, ndipo patapita nthawi anabweranso atakhala mfumu. Choncho cholinga cha kubweranso kwa Yesu, ndi kudzakhazikitsa ulamuliro wabwino kwa anthu.—Werengani Luka 19:11, 12.

Yesu adzabweretsa ulamuliro wabwino padzikoli

Kodi Yesu adzabweranso ndi thupi ngati la munthu? Kumbukirani kuti iye anaukitsidwa ndi thupi lauzimu. (1 Petulo 3:18) Kenako anapita kumwamba ndipo anakhala kudzanja lamanja la Mulungu. (Salimo 110:1) Patapita nthawi yaitali, Yesu anafika pafupi ndi “Wamasiku Ambiri,” yemwe ndi Yehova Mulungu, ndipo anam’patsa mphamvu zolamulira anthu. Choncho Yesu adzabwera, osati ngati munthu, koma monga Mfumu yosaoneka.—Werengani Danieli 7:13, 14.

Kodi Yesu akadzabweranso adzachita chiyani?

Yesu akadzabweranso ndi angelo ake mosaoneka, adzaweruza anthu. Adzawononga anthu oipa, koma anthu amene amam’mvera monga Mfumu yawo, adzawapatsa moyo wosatha.—Werengani Mateyu 25:31-33, 46.

Ulamuliro wa Yesu udzasintha dzikoli kukhala paradaiso. Komanso iye adzaukitsa anthu amene anamwalira kuti asangalale ndi moyo m’Paradaiso padziko lapansili.—Werengani Luka 23:42, 43.

Kuti mudziwe zambiri, werengani tsamba 73 mpaka 85 m’buku ili Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni?, lofalitsidwa ndi Mboni za Yehova

Mukhozanso kupanga dawunilodi bukuli pa www.jw.org

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena