Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w14 11/1 tsamba 3
  • Kodi Satana Alipodi?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Satana Alipodi?
  • Nsanja ya Olonda—2014
  • Nkhani Yofanana
  • Satana
    Galamukani!—2013
  • Khalani Maso Satana Akufuna Kukumezani
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Kodi Satana Ndani? Kodi Alikodi?
    Galamukani!—2007
  • Kodi Mumamudziwa Bwino Mdani Wanu?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2018
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2014
w14 11/1 tsamba 3

NKHANI YA PACHIKUTO | KODI SATANA ALIPODI?

Kodi Satana Alipodi?

Chithunzi cha Satana atagwetsedwa kuchokera kumwamba

Chipilala chomwe chili ku Madrid, m’dziko la Spain, chosonyeza Satana ngati mngelo woipa amene anagwetsedwa padziko lapansi

“Ndili mwana, ine ndi makolo anga tinkakhala ku El Salvador. Ndikachita mwano, mayi ankakonda kundiuza kuti, ‘Satana abwera kudzakutenga.’ Koma ine ndinkawayankha kuti, ‘Abwere! Ine sindiopa Satana chifukwa ndimakhulupirira Mulungu.’”—ROGELIO.

Kodi nanunso muli ndi maganizo ofanana ndi a Rogelio? Pa mfundo zomwe zili m’munsizi, ndi iti imene mukuona kuti ndi yolondola?

  • Satana ndi maganizo oipa amene munthu amakhala nawo mumtima mwake.

  • Satana alipodi, koma sachita chidwi kwenikweni ndi zochita za anthufe.

  • Satana ndi mngelo woipa yemwe amachititsa kuti anthu azichita zoipa.

Ena amaona kuti mfundo yolondola ndi yoyambayo, ena amati yachiwiriyo ndipo ena amati yolondola ndi yomalizayo. Koma kodi kudziwa zoona pa nkhaniyi n’kofunika? Ngati Satana kulibe, ndiye kuti amene amakhulupirira kuti alipo amakhulupirira zabodza. Ngati Satana alipodi koma sachita chidwi kwenikweni ndi zochita za anthufe, ndiye kuti anthu amene amamuopa, amangoopa njokaluzi. Komanso ngati Satana ndi mngelo woipa, yemwe amachititsa kuti anthu azichita zoipa, ndiye kuti ndi woopsa kwambiri kuposa mmene ambiri amaganizira.

Tiyeni tione zimene Mawu a Mulungu amanena pa mafunso otsatirawa: Kodi Satana ndi ndani? Kodi ndi maganizo oipa amene amakhala mumtima mwa munthu kapena ndi mngelo woipa? Ngati alipodi, kodi ndi woopsa? Nanga mungatani kuti mudziteteze?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena