Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w15 6/1 tsamba 16
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Nkhani Yofanana
  • Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
    Nsanja ya Olonda—2014
  • Phunzitsani Ana Anu kukonda Yehova
    Nsanja ya Olonda—2007
  • Makolo, Muzithandiza Ana Anu Kuti Azikonda Yehova
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2022
  • Mungatani Kuti Aliyense Azisangalala M’banja Lanu?​—Mbali Yachiwiri
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
w15 6/1 tsamba 16

KUYANKHA MAFUNSO A M’BAIBULO

Kodi mungatani kuti mukhale makolo abwino?

Bambo ndi mwana wake akuyang’ana tombolombo

Kodi mumaphunzitsa ana anu kuti azikonda Mulungu?

Makolo akamakondana komanso kulemekezana, ana awo amakula bwino. (Akolose 3:14, 19) Makolo abwino amakonda ana awo komanso amawayamikira ngati mmene Yehova ankachitira ndi Mwana wake.—Werengani Mateyu 3:17.

Yehova, yemwe ndi Atate wakumwamba, amamvetsera atumiki ake ndipo amamvetsa mavuto awo. Inunso muyenera kutengera chitsanzo chake. Ana anu akamakuuzani zinazake, muyenera kumvetsera ngakhale mutakhala kuti simukugwirizana ndi zimene akunenazo. (Yakobo 1:19) Muyeneranso kuyesetsa kuti muzimvetsa mmene ana anuwo akumvera.—Werengani Numeri 11:11, 15.

Mungatani kuti ana anu akule bwino?

Makolonu muli ndi udindo wopatsa ana anu malamulo oti azitsatira. (Aefeso 6:1) Pa nkhani imeneyinso muyenera kutengera chitsanzo cha Yehova. Yehova amatikonda ndipo amatipatsa malamulo omveka bwino. Amatiuzanso zimene zingachitike tikapanda kutsatira malamulowo. (Genesis 3:3) Yehova satikakamiza kutsatira malamulo ake. Koma amatiuza kuti tikatsatira malamulowo, zinthu zidzatiyendera bwino.—Werengani Yesaya 48:18, 19.

Muziyesetsa kuthandiza ana anu kuti azikonda Mulungu. Zimenezi zingawathandize kuti azichita zabwino ngakhale inuyo kulibe. Mulungu amatiphunzitsa potipatsa chitsanzo. Nanunso muzisonyeza chitsanzo chabwino kuti ana anu aziphunzira mosavuta.—Werengani Deuteronomo 6:5-7; Aefeso 4:32; 5:1.

Kuti mudziwe zambiri, werengani mutu 14 m’buku ili lakuti Kodi Baibulo Limaphunzitsa Chiyani Kwenikweni? lofalitsidwa ndi a Mboni za Yehova.

Bukuli likupezekanso pa webusaiti yathu ya www.jw.org/ny

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena