Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 10/01 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki wathu wa Ufumu—2002
  • Zimene Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
km 10/01 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda Oct. 15

“Kodi pakufunika chiyani kuti dzikoli likhale labwino ndi lachimwemwe? [Yembekezerani yankho.] Anthu ayesa maboma osiyanasiyana kuti zinthu zisinthe. Koma onani maganizo a Mulungu pankhaniyi. [Ŵerengani Yeremiya 10:23.] Nkhani iyi ikutchula ‘Chimene Chidzabweretse Dziko Lachimwemwe,’ ndiponso momwe zimenezi zidzachitikire posachedwapa.”

Galamukani! Nov. 8

“Mungandivomereze kuti masiku ano anthu ali pamavuto kusiyana ndi kale, kodi si choncho? [Yembekezerani yankho.] Baibulo linaneneratu zimenezi. [Ŵerengani 2 Timoteo 3:1.] Anthu ambiri amapeza mavuto ochuluka m’moyo moti amadzipha. Magazini iyi ili ndi thandizo lenileni. Ikusonyeza momwe tingathetsere nkhaŵa ndi mmene tingasangalalire ndi moyo.”

Nsanja ya Olonda Nov. 1

Mukatha kutchula nkhani yomvetsa chisoni, funsani kuti: “N’chifukwa chiyani anthu amachita zinthu zoipa ngati zimenezi? Tonse tikudziŵa zabwino ndi zoipa, koma anthu akuchitabe zinthu zoipa. Chifukwa chiyani? [Akayankha, ŵerengani Chivumbulutso 12:9.] Magazini iyi ikufotokoza mmene tingadzitetezere mwa kuteteza chikumbumtima chathu.”

Galamukani! Nov. 8

“Mosakayikira mukuvomereza kuti tikukhala mu nthaŵi za mavuto. [Akayankha, ŵerengani 2 Timoteo 3:3.] Nthaŵi zambiri ‘ukali’ umachitika ndi m’banja momwe. Nkhani iyi yakuti, ‘Kuthandiza Akazi Amene Amamenyedwa ndi Amuna Awo,’ ili ndi uthenga wolimbikitsa. Mwina pali amene mungamuuze uthenga wolimbikitsa umenewu.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena