Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 3/04 tsamba 8
  • Nkhondo ya Apakavalo Imene Mukumenya Nawo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Nkhondo ya Apakavalo Imene Mukumenya Nawo
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Nkhani Yofanana
  • Tsoka Lachiwiri Linali Makamu a Asilikali Okwera Pamahatchi
    Mapeto Osangalatsa a Masomphenya a M’buku la Chivumbulutso
  • Mauthenga a Ungelo Kaamba ka Tsiku Lathu
    Nsanja ya Olonda—1988
  • Yafika Nthaŵi ya Chiweruzo cha Mulungu
    Nsanja ya Olonda—1989
  • Mfundo Zazikulu za M’buku la Chivumbulutso—Gawo 1
    Nsanja ya Olonda—2009
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
km 3/04 tsamba 8

Nkhondo ya Apakavalo Imene Mukumenya Nawo

1, 2. Kodi atumiki a Mulungu masiku ano akuthandiza bwanji kukwaniritsa masomphenya aulosi opezeka pa Chivumbulutso 9:13-19?

1 ‘Mngelo wachisanu ndi chimodzi anawomba lipenga lake.’ Kenako, ‘ankhondo apakavalo’ okwana “zikwi makumi aŵiri zochulukitsa zikwi khumi” anachita phokoso langati bingu. Limeneli si gulu la ankhondo wamba. “Mitu ya akavalo [ili] ngati mitu ya mikango.” Mkamwa mwawo mukutuluka moto, utsi, ndi sulfure ndipo “michira yawo ifanana ndi njoka.” N’chifukwa chake gulu la ankhondo lophiphiritsira limeneli lasakaza kwambiri. (Chiv. 9:13-19) Kodi mukudziŵa mmene mukuthandizira pokwaniritsa masomphenya aulosi wapadera umenewu?

2 Otsalira odzozedwa ndi anzawo, a nkhosa zina, amalengeza ziŵeruzo za Mulungu mogwirizana. Zimenezi zachititsa kuti Matchalitchi Achikristu aonekere poyera kuti ndi akufa mwauzimu. Tiyeni tipende mbali ziŵiri za masomphenya aulosi zimene zikusonyeza chifukwa chake ntchito ya atumiki a Mulungu ikuyenda bwino kwambiri.

3. Kodi mwaphunzitsidwa bwanji kuti mulankhule uthenga wa Mulungu mogwira mtima?

3 Ophunzitsidwa Ndiponso Okonzeka Kupereka Uthenga wa Mulungu: Mwa Sukulu ya Utumiki wa Mulungu ndiponso misonkhano ina yampingo, atumiki a Mulungu aphunzitsidwa kulankhula uthenga wa Mulungu mogwira mtima. Potsanzira Yesu ndi ophunzira ake, iwo amapita kukafunafuna anthu oyenera, amalalikira kulikonse kumene angapeze anthu. (Mat. 10:11; Marko 1:16; Luka 4:15; Mac. 20:18-20) Njira yopezeka m’Baibulo yochitira ulaliki imeneyi yakhala yothandiza kwambiri.

4. Ndi zida ziti zimene ofalitsa ambiri ali nazo zowathandiza pogwira ntchito yawo?

4 Atumiki achikristu agaŵira mamiliyoni ambiri a Mabaibulo, mabuku, mabulosha, ndiponso magazini pogwira ntchito ya Mulungu yolalikira. Zofalitsa zimenezi zilipo m’zinenero pafupifupi 400, zokhudza nkhani zambiri zosiyanasiyana ndiponso zolembedwa mosangalatsa anthu osiyanasiyana. Kodi mumagwiritsa ntchito bwino zida zimenezi?

5, 6. N’chiyani chimasonyeza kuti anthu a Yehova amathandizidwa ndi Mulungu?

5 Utsogoleri Ndiponso Thandizo Lochokera Kumwamba: Masomphenya aulosiwa akusonyezanso bwino kuti ntchito imene ankhondo apakavalo akuphiphiritsira imathandizidwa ndi Mulungu. (Chiv. 9:13-15) Ntchito yolalikira yapadziko lonse ikuchitika mwa mzimu wa Mulungu osati mwa nzeru kapena mphamvu za anthu. (Zek. 4:6) Yehova akugwiritsa ntchito angelo kutsogolera ntchito imeneyi. (Chiv. 14:6) Chotero, kuphatikiza pantchito imene Mboni zake zikugwira, Yehova akupereka thandizo lochokera kumwamba kuti akokere anthu ofatsa kwa iye.—Yoh. 6:45, 65.

6 Chifukwa chakuti anthu a Yehova aphunzitsidwa, akonzekera bwino kupereka uthenga wa Mulungu, ndiponso akugwira ntchito motsogoleredwa ndi angelo, ntchito yawo singaimitsidwe. Choncho tiyeni tipitirize kuchita mbali yathu pokwaniritsa masomphenya aulosi osangalatsa ameneŵa.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena