Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 7/04 tsamba 5
  • Khalani Oyera m’Makhalidwe Anu Onse

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Khalani Oyera m’Makhalidwe Anu Onse
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Nkhani Yofanana
  • “Khalani Ndi Khalidwe Labwino Pakati pa Anthu a M’dzikoli”
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2014
  • Masiku Atatu Otsitsimulidwa Mwauzimu
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
  • Dikirani Yehova
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Khalani Chitsanzo pa Ntchito Zabwino
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
km 7/04 tsamba 5

Khalani Oyera m’Makhalidwe Anu Onse

1. N’chifukwa chiyani n’kofunika kukhala oyera m’makhalidwe athu onse?

1 Monga atumiki a Mulungu woyera, Yehova, timayesetsa kukhala oyera m’makhalidwe athu onse. (1 Pet. 1:15, 16) Izi zikutanthauza kuti timayesetsa kutsatira miyezo ya Yehova m’mbali zonse za moyo wathu. Msonkhano wachigawo wa chaka chino utipatsa mpata wapadera wosonyeza khalidwe loyera.

2. Kodi tingasonyeze bwanji kuganizira ena pamene tikudya ku lesitilanti?

2 Ku Lesitilanti: Woperekera zakudya pa lesitilanti yapafupi ndi malo amsonkhano wina anati: “Mboni n’zosiyana ndi anthu ena. Zimalemekeza anthu ena.” Khalidwe labwino limaphatikizapo kusalankhula ndiponso kuseka mokuwa kumene kungasokoneze ena amene akudya. Ngakhale pamene tikudya ndi kumwa, timafuna kuchita zonse ku ulemerero wa Mulungu.—1 Akor. 10:31.

3. Kodi khalidwe labwino pamalo amsonkhano likuphatikizapo kuchita chiyani?

3 Pamsonkhano: Khalidwe labwino liyenera kuonekera makamaka pamalo amsonkhano. Chonde mverani malangizo a akalinde, kaya ndi koimika magalimoto kapena mu holo. (Aheb. 13:17) Mabanja ayenera kukhala pamodzi osati kusiya ana awo, ndi achinyamata a zaka zapakati pa 13 mpaka 19, kukhala m’timagulu ndi achinyamata anzawo. Musalumikize makina aliwonse ojambulira ku magetsi kapena ku zokuzira mawu za pamsonkhano ndipo muwagwiritse ntchito popanda kudodometsa nawo ena. Ngati mukufuna kujambula zithunzi mapulogalamu ali m’kati, musagwiritse ntchito fulashi. Matelefoni a m’manja achunidwe moti asadodometse ena. Mukaona kuti pachitika ngozi pamalowo, chonde dziŵitsani akalinde kapena Dipatimenti ya Chipatala. Pamakhala anthu odziŵa ntchito yachipatala pamalo amsonkhano omwe angathandize.

4. Kodi khalidwe lathu pamisonkhano yachigawo limalemekeza bwanji Mulungu?

4 Khalidwe lathu limatisiyanitsa ndi anthu ena ndiponso limalemekeza Mulungu wathu. (1 Pet. 2:12) Pamalo amsonkhano, zochita za Mboni za Yehova zidzakhala pachionetsero. Choncho, tsimikizani mtima kukhala oyera m’makhalidwe anu onse.

[Bokosi patsamba 5]

Sonyezani Khalidwe Loyera

◼ Yang’anirani kwambiri ana anu

◼ Ganizirani ena

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena