Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 12/04 tsamba 1
  • Thandizo Lanu Likufunika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Thandizo Lanu Likufunika
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Nkhani Yofanana
  • Atumiki Othandiza Amagwira Ntchito Yofunika Kwambiri
    Gulu Lochita Chifuniro cha Mulungu
  • Abale, Feserani Mzimu Ndipo Yesetsani Kuti Muyenerere Udindo
    Nsanja ya Olonda—2010
  • Abale Achinyamata, Kodi Mukuyesetsa Kuti Muyenerere Udindo mu Mpingo?
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2013
  • Thandizani Ena Kuti Ayenerere Maudindo
    Nsanja ya Olonda—2011
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
km 12/04 tsamba 1

Thandizo Lanu Likufunika

1 “Zikomo kwambiri chifukwa cha zonse zimene mumatichitira. Mumatithandiza kwambiri.” Ndemanga imeneyi ikusonyeza bwino mmene timayamikira akulu ndi atumiki otumikira. Popeza kuti gulu la Mulungu likupitirizabe kukula, pakufunika amuna okhwima mwauzimu kuti atumikire m’mipingo pafupifupi 100,000 imene ili padziko lonse. Ngati ndinu mbale wobatizidwa, thandizo lanu likufunika.

2 Kukalamira Udindo: Kodi muyenera kuchita chiyani pokalamira maudindo owonjezereka? (1 Tim. 3:1) Mwachidule, tinganene kuti muyenera kuonetsa chitsanzo chabwino m’mbali zonse za moyo wanu. (1 Tim. 4:12; Tito 2:6-8; 1 Pet. 5:3) Muzitenga nawo mbali mokwanira mu ntchito yolalikira ndi kuthandiza ena kuchitanso zomwezo. (2 Tim. 4:5) Muziganizira kwambiri okhulupirira anzanu. (Aroma 12:13) Muziphunzira Mawu a Mulungu mwakhama ndi kuyesetsa kukhala ndi luso la kuphunzitsa. (Tito 1:9; 1 Tim. 4:13) Ntchito iliyonse imene akulu angakupatseni muziichita mwakhama. (1 Tim. 3:10) Ngati ndinu mutu wa banja, ‘muziweruza bwino nyumba yanu.’—1 Tim. 3:4, 5, 12.

3 Kutumikira pa udindo winawake ndi ntchito yaikulu ndipo imafuna mzimu wodzipereka. (1 Tim. 5:17) Choncho, pokalamira udindo yesetsani kutumikira ena modzichepetsa. (Mat. 20:25-28; Yoh. 13:3-5, 12-17) Sinkhasinkhani za mtima umene Timoteo anali nawo ndipo yesetsani kum’tsanzira. (Afil. 2:20-22) Mofanana ndi iye, yesetsani kukhala ndi mbiri yabwino posonyeza khalidwe labwino. (Mac. 16:1, 2) Mukamayesetsa kukhala ndi makhalidwe auzimu ofunika kuti musamalire maudindo owonjezereka ndiponso mukamagwiritsa ntchito malangizo okuwongolerani amene ena angakupatseni, kupita patsogolo kwanu kudzaonekera kwa anthu onse.—1 Tim. 4:15.

4 Makolo, Phunzitsani Ana Anu Kuthandiza: Ana akhoza kuphunzira kukhala othandiza kuyamba adakali aang’ono. Aphunzitseni kukhala tcheru pamisonkhano, kulalikira, ndi kukhala ndi khalidwe labwino pa Nyumba ya Ufumu ndi kusukulu. Aphunzitseni kuti azikonda kutumikira ena, kuchita zinthu monga kuthandiza nawo kuyeretsa pa Nyumba ya Ufumu, kuthandiza okalamba, ndi ntchito zina. Aloleni kudzionera okha kuti ngati ali ndi mtima wopatsa adzapeza chimwemwe. (Mac. 20:35) Akaphunzitsidwa zinthu ngati zimenezi, zidzawathandiza kudzakhala apainiya, atumiki otumikira, ndi akulu m’tsogolo muno.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena